Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 1 Samueli 17:55
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 55 Sauli ataona Davide akupita kukakumana ndi Mfilisiti uja, anafunsa Abineri,+ mkulu wa asilikali, kuti: “Kodi ameneyu ndi mwana+ wa ndani,+ Abineri?” Poyankha Abineri anati: “Ndikulumbira pali moyo wanu mfumu, ine sindikudziwa ngakhale pang’ono!”

  • 1 Samueli 20:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 Koma poyankha Davide analumbira+ kuti: “Bambo ako ayenera kuti akudziwa ndithu kuti iweyo umandikonda.+ Pa chifukwa chimenechi iwo adzanena kuti, ‘Musamuuze zimenezi Yonatani kuti zingamupweteketse mtima.’ Moti ndikunenetsa, pali Yehova Mulungu wamoyo,+ komanso pali moyo wako,+ imfa ili pafupi kwambiri ndi ine!”+

  • 2 Samueli 11:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 Pamenepo Uriya anayankha Davide kuti: “Likasa,+ Isiraeli ndi Yuda akukhala m’misasa, ndipo mbuyanga Yowabu pamodzi ndi atumiki anu mbuyanga+ ali mumsasa kuthengo. Ndiye ine ndikalowe m’nyumba yanga kukadya chakudya, kumwa ndi kugona ndi mkazi wanga?+ Ndithu, pali inu ndi moyo wanu,+ sindingachite zimenezo.”

  • 2 Mafumu 2:2
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 2 Kenako Eliya anauza Elisa kuti: “Iweyo khala apa, pakuti ine Yehova wandituma ku Beteli.” Koma Elisa anati: “Pali Yehova Mulungu wamoyo+ ndiponso pali moyo wanu,+ sindikusiyani.”+ Choncho iwo anapita ku Beteli.+

  • 2 Mafumu 4:30
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 30 Pamenepo mayi wa mwanayo anati: “Pali Yehova Mulungu wamoyo+ ndiponso pali moyo wanu+ sindikusiyani.”+ Choncho Elisa ananyamuka n’kupita pamodzi ndi mayiyo.

  • Mlaliki 9:5
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 5 Pakuti amoyo amadziwa kuti adzafa,+ koma akufa sadziwa chilichonse.+ Iwo salandiranso malipiro alionse, chifukwa zonse zimene anthu akanawakumbukira nazo zaiwalika.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena