5 Usaziweramire kapena kuzitumikira,+ chifukwa ine Yehova Mulungu wako, ndine Mulungu wofuna kuti anthu azidzipereka kwa ine ndekha,*+ wolanga ana, zidzukulu ndi ana a zidzukuluzo, chifukwa cha zolakwa za abambo a anthu odana ndi ine.+
29 Mlandu umenewu ubwerere pamutu+ pa Yowabu ndi pa nyumba yonse ya bambo ake. M’nyumba ya Yowabu+ simudzasowa munthu wa nthenda yakukha kumaliseche+ ndiponso wakhate.+ Simudzasowanso mwamuna wogwira ndodo yowombera nsalu,+ wokanthidwa ndi lupanga kapena wosowa mkate!”+
21Tsopano m’masiku a Davide kunagwa njala+ zaka zitatu zotsatizana. Choncho Davide anafunsira kwa Yehova, ndipo Yehova anamuuza kuti: “Sauli pamodzi ndi nyumba yake ali ndi mlandu wa magazi chifukwa anapha Agibeoni.”+