Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 2 Mbiri 36:16
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 16 Koma iwo ankangonyogodola+ amithenga a Mulungu woona, kunyoza mawu ake+ ndi kuseka+ aneneri ake, mpaka kufika poti panalibenso chiyembekezo choti angathe kuchiritsidwa.+ Kenako mkwiyo+ wa Yehova unawagwera.

  • Nehemiya 9:33
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 33 Inu ndinu wolungama+ pa zinthu zonse zimene zatichitikira, pakuti inu mwachita zinthu mokhulupirika+ koma ife tachita zinthu zoipa.+

  • Yeremiya 30:14
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 14 Achigololo onse amene anali kukukonda kwambiri akuiwala.+ Iwo sakukufunafunanso. Ndakumenya ndi mkwapulo+ ngati mdani ndipo ndakulanga ngati munthu wankhanza+ chifukwa cha kuchuluka kwa zolakwa zako.+ Machimo ako achuluka kwambiri.+

  • Maliro 1:18
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 18 Yehova ndi wolungama,+ koma ine ndapandukira+ mawu a pakamwa pake.

      Anthu nonsenu, tamverani mawu anga, ndipo muone ululu umene ndikumva.

      Anamwali anga ndi anyamata anga atengedwa kupita ku ukapolo.+

  • Ezekieli 8:17
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 17 Iye anapitiriza kundiuza kuti: “Iwe mwana wa munthu, kodi waona zimenezi? Kodi a nyumba ya Yuda akuona ngati ndi chinthu chaching’ono kuchita zinthu zonyansa zimene akuchita panozi? Kodi akufunanso kuti adzaze dzikoli ndi chiwawa+ n’kundikwiyitsa kachiwiri? Kodi waonanso kuti iwowo akulozetsa nthambi* kumphuno kwanga?

  • Danieli 9:7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 7 Inu Yehova ndinu wolungama, koma ife manyazi aphimba nkhope zathu lero.+ Manyazi aphimba nkhope za amuna a mu Yuda, anthu a ku Yerusalemu ndi anthu onse a ku Isiraeli, amene ali pafupi ndiponso amene ali kumayiko onse akutali kumene munawabalalitsira chifukwa cha zinthu zosakhulupirika zimene anakuchitirani.+

  • Danieli 9:16
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 16 Inu Yehova, nthawi zonse mumachita zinthu zolungama.+ Chonde, chotsani mkwiyo wanu waukulu pa Yerusalemu, phiri lanu loyera.+ Pakuti chifukwa cha machimo athu ndi zolakwa za makolo athu,+ Yerusalemu ndi anthu anu takhala chinthu chotonzedwa ndi anthu onse otizungulira.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena