-
Salimo 89:50Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
50 Inu Yehova, kumbukirani chitonzo chimene chagwera atumiki anu.+
Kumbukirani kuti ndanyamula pachifuwa panga chitonzo cha mitundu yambiri ya anthu.+
-
Yeremiya 18:18Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
18 Iwo anapitiriza kunena kuti: “Bwerani anthu inu, timukonzere chiwembu Yeremiya,+ pakuti chilamulo sichidzachoka pakamwa pa ansembe athu.+ Anthu athu anzeru sadzaleka kupereka malangizo ndiponso aneneri athu sadzaleka kulosera.+ Tabwerani, tiyeni timuukire ndi malilime athu+ ndipo tisamvere mawu ake ngakhale pang’ono.”
-
-
-