-
Yeremiya 30:10Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
10 “Koma iwe Yakobo mtumiki wanga usachite mantha, iwe Isiraeli usagwidwe ndi mantha,”+ watero Yehova. “Pakuti ine ndikukupulumutsa kuchokera kutali ndipo ndikupulumutsanso ana ako kuchokera kudziko limene anatengedwa kukakhala akapolo.+ Yakobo adzabwerera ndipo adzakhala mosatekeseka komanso mopanda zosokoneza. Sipadzakhala womuopsa.”+
-
-
Ezekieli 36:4Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
4 Tsopano inu mapiri a ku Isiraeli,+ tamverani mawu a Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa. Yehova, Ambuye Wamkulu Koposa, walankhula ndi mapiri, zitunda, mitsinje, zigwa ndi malo owonongedwa amene ndi mabwinja.+ Walankhulanso ndi mizinda yopanda anthu imene anthu otsala a mitundu ina anaitenga kukhala yawo. Anthuwo anakhala moizungulira ndipo amainyoza.+
-