27 “‘Koma iwe Yakobo mtumiki wanga, usaope ndipo usagwidwe ndi mantha, iwe Isiraeli.+ Pakuti ine tsopano ndikukupulumutsa kuchokera kutali. Mbewu yako ndikuipulumutsa kuchokera m’dziko limene iwo anali akapolo.+ Yakobo adzabwerera ndi kukhala mwabata ndiponso mosatekeseka, popanda womuopsa.+