20 Yehova anapitiriza kulankhula ndi Aroni, kuti: “Iwe udzakhala wopanda cholowa m’dziko mwawo, ndipo sudzapatsidwa gawo lililonse pakati pawo.+ Ine ndine gawo lako ndi cholowa chako pakati pa ana a Isiraeli.+
14 Fuko la Alevi lokha ndi limene sanalipatse cholowa cha malo.+ Cholowa chawo ndicho nsembe zotentha ndi moto+ zoperekedwa kwa Yehova Mulungu wa Isiraeli, monga mmene anawalonjezera.+
4 Malo oyerawa adzakhale gawo la ansembe m’dzikoli.+ Ansembewo ndi atumiki a pamalo opatulika ndipo amayandikira kwa Yehova ndi kumutumikira.+ Malo amenewa adzakhale awo kuti adzamangepo nyumba zawo. Adzakhalenso malo opatulika omangapo nyumba yopatulika.