Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Levitiko 26:44
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 44 Koma ngakhale kuti padzachitika zonsezi, pamene iwo akukhala m’dziko la adani awo, sindidzawakana+ kapena kunyansidwa nawo+ moti n’kuwafafaniziratu, kuphwanya pangano langa+ ndi iwo, chifukwa ine ndine Yehova Mulungu wawo.

  • Deuteronomo 30:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 Yehova Mulungu wanu adzabweza kwawo anthu a mtundu wanu amene anagwidwa ndi kupita kudziko lina,+ ndipo adzakumverani chifundo+ n’kukusonkhanitsaninso pamodzi kuchokera pakati pa anthu onse kumene Yehova Mulungu wanu anakubalalitsirani.+

  • 2 Mafumu 24:15
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 15 Chotero iye anatengera Yehoyakini+ ku Babulo.+ Anatenga ku Yerusalemu mayi a mfumuyo,+ akazi ake, nduna za panyumba yake,+ ndi akuluakulu a m’dzikolo, n’kuwapititsa ku Babulo.

  • Salimo 44:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 Mwatipereka kwa adani athu kuti atidye ngati nkhosa,+

      Ndipo mwatimwaza pakati pa anthu a mitundu ina.+

  • Yeremiya 24:5
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 5 “Yehova Mulungu wa Isiraeli wanena kuti, ‘Anthu otengedwa ku Yuda kupita ku ukapolo kudziko la Akasidi ndidzawaona ngati nkhuyu zabwino zimenezi. Ndidzawatumiza kudziko la Akasidi+ kuchoka m’dziko lino m’njira yabwino.+

  • Yeremiya 30:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 “Pakuti ine ndili ndi iwe kuti ndikupulumutse,”+ watero Yehova. “Ndidzawononga anthu a mitundu yonse ya kumene ndinakubalalitsirani,+ koma iwe sindidzakuwononga.+ Ndidzakuwongolera pa mlingo woyenera chifukwa sindidzakusiya osakulanga.”+

  • Yeremiya 31:10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Inu mitundu ya anthu, imvani mawu a Yehova, ndipo mulengeze mawuwo pazilumba zakutali,+ kuti: “Amene wamwaza Isiraeli ndiye adzamusonkhanitsanso+ ndipo adzamusunga mmene m’busa amasungira nkhosa zake.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena