13 Mulungu wa Abulahamu, wa Isaki ndi wa Yakobo,+ Mulungu wa makolo athu, ndi amene walemekeza+ Mtumiki+ wake Yesu, amene inu munamupereka+ ndi kumukana pamaso pa Pilato, Pilatoyo akufuna kumumasula.+
26 Pakuti mkulu wa ansembe ngati ameneyu ndiyedi wotiyenerera.+ Iye ndi wokhulupirika,+ wosalakwa,+ wosaipitsidwa,+ wosiyana ndi anthu ochimwa,+ ndipo wakwera pamwamba kwambiri kuposa kumwamba.+