Ekisodo 15:11 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 11 Ndi mulungu uti amene angafanane nanu, inu Yehova?+ Mumasonyeza kuti ndinu woyera koposa,+ ndani angafanane ndi inu? Ndinu woyenera kuopedwa ndi kukuimbirani nyimbo zotamanda. Inu mumachita zodabwitsa.+ Deuteronomo 4:35 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 35 Inuyo mwasonyezedwa zinthu zimenezi kuti mudziwe kuti Yehova ndi Mulungu woona.+ Palibenso Mulungu wina kupatulapo iyeyo.+ Salimo 73:25 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 25 Winanso ndi ndani kumwambako amene angandithandize? Ndipo chifukwa chakuti inu muli ndi ine, palibenso chimene ndimalakalaka padziko lapansi.+ Salimo 86:8 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 8 Inu Yehova, palibe mulungu wina amene angafanane ndi inu,+Palibe aliyense amene wachita zinthu zofanana ndi zimene inu mwachita.+ Salimo 89:6 Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika 6 Ndi ndani kumwamba amene angafanane ndi Yehova?+ Ndi ndani pakati pa ana a Mulungu+ amene ndi wofanana ndi Yehova?
11 Ndi mulungu uti amene angafanane nanu, inu Yehova?+ Mumasonyeza kuti ndinu woyera koposa,+ ndani angafanane ndi inu? Ndinu woyenera kuopedwa ndi kukuimbirani nyimbo zotamanda. Inu mumachita zodabwitsa.+
35 Inuyo mwasonyezedwa zinthu zimenezi kuti mudziwe kuti Yehova ndi Mulungu woona.+ Palibenso Mulungu wina kupatulapo iyeyo.+
25 Winanso ndi ndani kumwambako amene angandithandize? Ndipo chifukwa chakuti inu muli ndi ine, palibenso chimene ndimalakalaka padziko lapansi.+
8 Inu Yehova, palibe mulungu wina amene angafanane ndi inu,+Palibe aliyense amene wachita zinthu zofanana ndi zimene inu mwachita.+
6 Ndi ndani kumwamba amene angafanane ndi Yehova?+ Ndi ndani pakati pa ana a Mulungu+ amene ndi wofanana ndi Yehova?