Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Genesis 49:10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Ndodo yachifumu sidzachoka kwa Yuda,+ ndiponso chibonga cha wolamulira sichidzachoka pakati pa mapazi ake, mpaka Silo* atabwera.+ Ndipo mitundu ya anthu idzamumvera.+

  • 1 Mafumu 8:20
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 20 Yehova wakwaniritsa zimene analonjeza, chifukwa ndalowa mʼmalo mwa bambo anga Davide ndipo ndakhala pampando wachifumu wa Isiraeli, mogwirizana ndi zimene Yehova analonjeza. Komanso ndamanga nyumba ya dzina la Yehova Mulungu wa Isiraeli.+

  • 1 Mbiri 17:11-14
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 Ukadzamwalira nʼkugona mʼmanda ndi makolo ako, ndidzachititsa kuti mbadwa* yako, mmodzi wa ana ako,+ akhale mfumu ndipo ndidzachititsa kuti ufumu wake ukhazikike.+ 12 Iye ndi amene adzandimangire nyumba+ ndipo ndidzakhazikitsa mpando wake wachifumu mpaka kalekale.+ 13 Ine ndidzakhala bambo ake ndipo iye adzakhala mwana wanga.+ Sindidzamuchotsera chikondi changa chokhulupirika+ ngati mmene ndinachitira kwa munthu yemwe analipo iwe usanakhalepo.+ 14 Ndidzamuchititsa kuti akhale woyangʼanira nyumba yanga ndi ufumu wanga mpaka kalekale,+ ndipo mpando wake wachifumu udzakhalapo mpaka kalekale.”’”+

  • Salimo 132:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 Yehova walumbira kwa Davide.

      Ndithudi sadzalephera kukwaniritsa mawu ake akuti:

      “Ndidzaika pampando wako wachifumu

      Mmodzi wa ana ako.*+

  • Yesaya 9:7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  7 Ulamuliro* wake udzafika kutali

      Ndipo mtendere sudzatha,+

      Pampando wachifumu wa Davide+ ndiponso mu ufumu wake

      Kuti iye achititse ufumuwo kukhazikika+ ndiponso kukhala wolimba

      Pogwiritsa ntchito chilungamo+ ndiponso mtima wowongoka,+

      Kuyambira panopa mpaka kalekale.

      Yehova wa magulu ankhondo akumwamba adzachita zimenezi modzipereka kwambiri.

  • Yesaya 11:1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 Nthambi+ idzaphuka pachitsa cha Jese,+

      Ndipo mphukira+ yotuluka pamizu yake idzabereka zipatso.

  • Mateyu 21:9
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 Komanso gulu la anthu limene linali patsogolo pake ndi mʼmbuyo mwake linkafuula kuti: “Mʼpulumutseni Mwana wa Davide!+ Wodalitsidwa ndi amene akubwera mʼdzina la Yehova!*+ Mʼpulumutseni kumwambamwambako!”+

  • Mateyu 22:42
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 42 “Mukuganiza bwanji za Khristu? Kodi ndi mwana wa ndani?” Iwo anayankha kuti: “Ndi mwana wa Davide.”+

  • Luka 1:32, 33
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 32 Ameneyu adzakhala wamkulu+ ndipo adzatchedwa Mwana wa Wamʼmwambamwamba.+ Yehova* Mulungu adzamupatsa mpando wachifumu wa Davide atate wake.+ 33 Iye adzalamulira monga Mfumu panyumba ya Yakobo kwamuyaya ndipo Ufumu wake sudzatha.”+

  • Yohane 7:42
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 42 Kodi si paja lemba limanena kuti Khristu adzachokera mwa ana a Davide+ komanso ku Betelehemu,+ mudzi umene Davide ankakhala?”+

  • Machitidwe 2:30
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 30 Iye anali mneneri ndipo ankadziwa kuti Mulungu anamulonjeza polumbira, kuti pampando wake wachifumu adzakhazikapo mmodzi wa mbadwa zake.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena