Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Ekisodo 30:12-16
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 “Ukamachita kalembera wa ana a Isiraeli,+ aliyense azipereka dipo la moyo wake kwa Yehova pa nthawi imene ukuwawerengayo. Azichita zimenezi kuti mliri usawagwere pochita kalemberayo. 13 Anthu onse amene awerengedwa azipereka zinthu izi: hafu ya sekeli* yofanana ndi sekeli yakumalo oyera.*+ Magera* 20 amakwana sekeli imodzi. Hafu ya sekeli ndi chopereka kwa Yehova.+ 14 Aliyense amene wawerengedwa, kuyambira wa zaka 20 kupita mʼtsogolo azipereka chopereka kwa Yehova.+ 15 Mukamapereka kwa Yehova chopereka chophimba machimo kuti muwombole moyo wanu, anthu olemera asapereke zochuluka, ndipo osauka asapereke zosakwana hafu ya sekeli.* 16 Uzilandira ndalama zasiliva zophimbira machimo kwa Aisiraeli nʼkuzipereka kuti zikagwiritsidwe ntchito pa utumiki wapachihema chokumanako. Ndalama zimenezi zidzathandiza kuti Yehova azikumbukira Aisiraeli komanso zidzaphimba machimo anu kuti muwombole moyo wanu.”

  • Nehemiya 10:32
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 32 Kuwonjezera pamenepo, tinalonjeza kuti chaka chilichonse aliyense azipereka ndalama zasiliva zolemera magalamu 4* kuti akazigwiritse ntchito pa utumiki wapanyumba* ya Mulungu wathu.+

  • Mateyu 17:24
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 24 Atafika ku Kaperenao, anthu okhometsa msonkho wa madalakima awiri anapita kwa Petulo nʼkumufunsa kuti: “Kodi mphunzitsi wanu amapereka madalakima awiri* a msonkho?”+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena