19 Mukaiwala mtolo wa tirigu pokolola mʼmunda mwanu, musamabwerere kukatenga mtolowo. Muzisiyira mlendo wokhala mʼdziko lanu, mwana wamasiye ndi mkazi wamasiye.+ Muzichita zimenezi kuti Yehova Mulungu wanu akudalitseni pa chilichonse chimene mukuchita.+