17 Ine ndinakwiya chifukwa cha machimo amene ankachita pofuna kupeza phindu mwachinyengo,+
Choncho ndinamulanga, ndinabisa nkhope yanga ndipo ndinakwiya.
Koma iye anapitiriza kuyenda ngati wopanduka,+ ankangotsatira zofuna za mtima wake.
18 Ine ndaona njira zake,
Koma ndidzamuchiritsa+ nʼkumutsogolera,+
Ndipo ndidzayambiranso kumutonthoza,+ iyeyo ndi anthu ake amene akulira.”+