Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Deuteronomo 30:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 Yehova Mulungu wanu adzabweza kwawo anthu a mtundu wanu amene anagwidwa nʼkupita kudziko lina,+ ndipo adzakuchitirani chifundo+ nʼkukusonkhanitsaninso pamodzi kuchokera pakati pa anthu onse kumene Yehova Mulungu wanu anakubalalitsirani.+

  • Salimo 30:5
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  5 Chifukwa mkwiyo wa Mulungu sukhalitsa pa munthu,+

      Koma munthu amene wasangalala naye* amamukomera mtima kwa moyo wake wonse.+

      Munthu akhoza kulira usiku, koma mʼmawa amafuula mosangalala.+

  • Yesaya 54:7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  7 “Ndinakusiya kwa kanthawi kochepa,

      Koma ndidzakusonkhanitsa pamodzi mwachifundo chachikulu.+

  • Yesaya 57:17, 18
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 17 Ine ndinakwiya chifukwa cha machimo amene ankachita pofuna kupeza phindu mwachinyengo,+

      Choncho ndinamulanga, ndinabisa nkhope yanga ndipo ndinakwiya.

      Koma iye anapitiriza kuyenda ngati wopanduka,+ ankangotsatira zofuna za mtima wake.

      18 Ine ndaona njira zake,

      Koma ndidzamuchiritsa+ nʼkumutsogolera,+

      Ndipo ndidzayambiranso kumutonthoza,+ iyeyo ndi anthu ake amene akulira.”+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena