Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Deuteronomo 28:49, 50
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 49 Yehova adzatumiza mtundu wakutali+ kuchokera kumalekezero adziko lapansi kuti udzakuukireni. Mtunduwo udzakuukirani mofulumira kwambiri ngati mmene chiwombankhanga chimagwirira nyama.+ Mtundu umenewo chilankhulo chake simudzachimva,+ 50 mtundu wooneka moopsa umene sudzamvera chisoni munthu wachikulire kapena kuchitira chifundo mnyamata.+

  • Yeremiya 4:13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 13 Taonani! Mdani adzabwera ngati mitambo yamvula,

      Ndipo magaleta ake ali ngati mphepo yamkuntho.+

      Mahatchi ake ndi aliwiro kuposa ziwombankhanga.+

      Tsoka latigwera chifukwa tawonongedwa.

  • Maliro 4:19
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 19 Anthu amene ankatithamangitsa anali aliwiro kuposa ziwombankhanga zouluka mʼmwamba.+

      Iwo anatithamangitsa mʼmapiri. Anatibisalira mʼchipululu.

  • Habakuku 1:6
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  6 Ine ndikubweretsa Akasidi,+

      Mtundu wankhanza ndiponso waphuma.

      Umene umathamanga mʼmadera ambiri apadziko lapansi,

      Kukalanda nyumba zimene si zawo.+

  • Habakuku 1:8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  8 Mahatchi* ake ndi aliwiro kuposa akambuku,

      Ndi oopsa kuposa mimbulu usiku.+

      Mahatchi ake ankhondo amathamanga kwambiri.

      Mahatchi awo amachokera kutali.

      Ndipo amauluka ngati chiwombankhanga chimene chikuthamanga kuti chikapeze chakudya.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena