Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 1 Mafumu 17:9, 10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 “Nyamuka, upite ku Zarefati mʼdziko la Sidoni ukakhale kumeneko. Ine ndikalamula mayi wamasiye kuti azikakupatsa chakudya.”+ 10 Choncho Eliya ananyamuka nʼkupita ku Zarefati. Atafika pageti la mzindawo anaona mayi wamasiye akutola nkhuni. Ndiyeno anamuitana nʼkumuuza kuti: “Mundipatseko madzi pangʼono mʼkapu kuti ndimwe.”+

  • 1 Mafumu 17:20-23
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 20 Kenako anafuulira Yehova kuti: “Inu Yehova Mulungu wanga,+ kodi mukuchitiranso zoipa mayi wamasiye amene ndikukhala nayeyu pomuphera mwana wake?” 21 Ndiyeno anakumbatira mwanayo katatu ali pabedipo nʼkufuulira Yehova kuti: “Inu Yehova Mulungu wanga, chonde chititsani kuti moyo wa mwanayu ubwerere.” 22 Yehova anamva pemphero la Eliya+ ndipo moyo wa mwanayo unabwerera moti anakhalanso wamoyo.+ 23 Eliya anatenga mwanayo nʼkutsika naye kuchokera mʼchipinda chapadenga chija ndipo anapita naye kwa mayi ake. Ndiyeno anati: “Mwana wanu uja tsopano ali moyo.”+

  • 2 Mafumu 4:8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 8 Tsiku lina Elisa anapita ku Sunemu.+ Kumeneko kunali mayi wina wodziwika. Mayiyo anaumiriza Elisa kuti adye chakudya.+ Nthawi zonse Elisa akamadutsa, ankaima kunyumba kwa mayiyo kuti adye chakudya.

  • 2 Mafumu 4:13-17
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 13 Ndiyeno Elisa anauza Gehazi kuti: “Muuze kuti, ‘Mwavutika ndi kutisamalira,+ kodi tingakuchitireni chiyani?+ Kodi pali chinachake choti tikakunenereni kwa mfumu,+ kapena kwa mkulu wa asilikali?’” Koma mayiyo anayankha kuti: “Ayi, palibe. Ndikukhala mwamtendere ndi anthu a mtundu wanga.” 14 Elisa anati: “Ndiye timuchitire chiyani?” Gehazi anayankha kuti: “Mayiyutu alibe mwana wamwamuna+ ndipo mwamuna wake ndi wokalamba.” 15 Nthawi yomweyo Elisa anati: “Muitane.” Choncho Gehazi anamuitana ndipo mayiyo anaima pakhomo. 16 Ndiyeno Elisa anati: “Chaka chamawa nthawi ngati yomwe ino mudzakhala ndi mwana wamwamuna.”+ Koma mayiyo atamva anati: “Ayi mbuyanga, munthu wa Mulungu woona! Musandinamize ine kapolo wanu.”

      17 Komabe, mayiyo anakhala ndi pakati nthawi ngati yomweyo chaka chotsatira ndipo anabereka mwana wamwamuna mogwirizana ndi zimene Elisa anamuuza.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena