Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Mateyu 20:17-19
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 17 Ali panjira yopita ku Yerusalemu, Yesu anatengera pambali ophunzira ake 12 aja nʼkuwauza kuti:+ 18 “Tsopano tikupita ku Yerusalemu ndipo Mwana wa munthu akaperekedwa kwa ansembe aakulu ndi alembi. Iwo akamuweruza kuti aphedwe+ 19 ndipo akamupereka kwa anthu a mitundu ina kuti amuchitire chipongwe, kumukwapula ndi kumupachika pamtengo+ ndipo pa tsiku lachitatu adzaukitsidwa.”+

  • Maliko 8:31
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 31 Komanso anayamba kuwaphunzitsa kuti Mwana wa munthu akuyenera kukumana ndi mavuto ambiri ndiponso kukanidwa ndi akulu, ansembe aakulu ndi alembi. Ndipo adzaphedwa+ nʼkuukitsidwa patapita masiku atatu.+

  • Maliko 9:31
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 31 Chifukwa iye ankaphunzitsa ophunzira ake nʼkuwauza kuti: “Mwana wa munthu adzaperekedwa mʼmanja mwa anthu ndipo adzamupha.+ Koma ngakhale adzamuphe, adzauka patatha masiku atatu.”+

  • Luka 9:22
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 22 Kenako anati: “Mwana wa munthu akuyenera kukumana ndi mavuto ambiri ndiponso kukanidwa ndi akulu, ansembe aakulu ndi alembi. Ndipo adzaphedwa+ nʼkuukitsidwa patapita masiku atatu.”+

  • Luka 18:31-33
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 31 Kenako anatengera pambali ophunzira 12 aja nʼkuwauza kuti: “Tamverani! Tsopano tikupita ku Yerusalemu ndipo zonse zimene zinalembedwa ndi aneneri zokhudza Mwana wa munthu zikakwaniritsidwa.+ 32 Mwachitsanzo, akamupereka kwa anthu a mitundu ina+ ndipo akamuchitira chipongwe,+ kumunyoza komanso kumulavulira.+ 33 Akakamaliza kumukwapula akamupha,+ koma pa tsiku lachitatu iye adzauka.”+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena