Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Deuteronomo 21:22, 23
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 22 Ngati munthu wachita tchimo loyenera chiweruzo choti aphedwe,+ ndiyeno munthuyo waphedwa, ndipo mwamupachika pamtengo,+ 23 mtembo wake usamakhale pamtengopo usiku wonse.+ Mʼmalomwake, muzionetsetsa kuti mwamuika mʼmanda tsiku lomwelo, chifukwa munthu aliyense wopachikidwa pamtengo ndi wotembereredwa ndi Mulungu.+ Musamaipitse dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani kuti likhale cholowa chanu.”+

  • Mateyu 27:57, 58
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 57 Tsopano madzulo kwambiri, kunabwera munthu wina wachuma wa ku Arimateya, dzina lake Yosefe, amenenso anakhala wophunzira wa Yesu.+ 58 Iye anapita kwa Pilato kukapempha mtembo wa Yesu+ ndipo Pilato analamula kuti amupatse mtembowo.+

  • Luka 23:50-52
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 50 Ndiyeno panali mwamuna wina dzina lake Yosefe, amene anali wa mʼKhoti Lalikulu la Ayuda. Munthu ameneyu anali wabwino komanso wolungama.+ 51 (Iye sanavomereze chiwembu chawo komanso zimene anachita.) Yosefe anali wochokera ku Arimateya, mzinda wa Ayudeya ndipo ankayembekezera Ufumu wa Mulungu. 52 Iye anapita kwa Pilato kukapempha mtembo wa Yesu.

  • Yohane 19:38
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 38 Pambuyo pa zinthu zimenezi, Yosefe wa ku Arimateya, amene anali wophunzira wachinsinsi wa Yesu chifukwa ankaopa Ayuda,+ anapempha Pilato kuti akachotse mtembo wa Yesu ndipo Pilato anamupatsa chilolezo. Choncho anafika nʼkuchotsa mtembowo.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena