Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Mateyu 14:3-5
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 Herode* anagwira Yohane nʼkumumanga ndipo anamutsekera mʼndende chifukwa cha Herodiya, mkazi wa mchimwene wake Filipo amene Herodeyo anakwatira.+ 4 Anachita zimenezi chifukwa Yohane ankamuuza kuti: “Nʼzosaloleka kuti mutenge mkazi ameneyu kukhala mkazi wanu.”+ 5 Komabe, ngakhale kuti Herode ankafuna kupha Yohane, ankaopa gulu la anthu chifukwa iwo ankakhulupirira kuti anali mneneri.+

  • Maliko 6:17-20
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 17 Ananena zimenezi chifukwa Herodeyo anatumiza anthu kuti akagwire Yohane nʼkumumanga ndipo anamutsekera mʼndende chifukwa cha Herodiya, mkazi wa mchimwene wake Filipo amene Herodeyo anakwatira.+ 18 Anachita zimenezi chifukwa Yohane ankauza Herode kuti: “Nʼzosaloleka kuti mutenge mkazi wa mchimwene wanu.”+ 19 Choncho Herodiya anamusungira chidani mumtima ndipo ankafuna kumupha, koma sanakwanitse kuchita zimenezo. 20 Herode ankaopa Yohane chifukwa ankadziwa kuti ndi munthu wolungama komanso woyera,+ choncho ankamuteteza. Atamva zimene ankanena anathedwa nzeru, komabe anapitiriza kumumvetsera mosangalala.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena