Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Mateyu 14:14-17
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 14 Yesu atatsika mʼngalawayo anaona gulu lalikulu la anthu ndipo anawamvera chisoni+ nʼkuwachiritsira anthu awo odwala.+ 15 Koma chakumadzulo ophunzira ake anabwera kwa iye nʼkunena kuti: “Kuno nʼkopanda anthu ndipo nthawi yatha, auzeni anthuwa kuti anyamuke, apite mʼmidzimo kuti akagule chakudya choti adye.”+ 16 Koma Yesu anawayankha kuti: “Palibe chifukwa choti apitire. Inuyo muwapatse chakudya.” 17 Iwo anamuuza kuti: “Tilibe chilichonse pano, kupatulapo mitanda 5 ya mkate ndi nsomba ziwiri zokha basi.”

  • Maliko 6:35-38
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 35 Tsopano kunja kunayamba kuda ndipo ophunzira ake anabwera kwa iye nʼkunena kuti: “Kuno nʼkopanda anthu ndipo nthawi yatha.+ 36 Auzeni anthuwa kuti anyamuke, apite mʼmidzi yapafupi ndi mʼmadera ozungulira kuti akagule chakudya choti adye.”+ 37 Koma iye anawayankha kuti: “Inuyo muwapatse chakudya.” Yesu atanena zimenezi iwo anamufunsa kuti: “Kodi tipite kukagula mitanda ya mkate ya ndalama zokwana madinari* 200 nʼkuipereka kwa anthuwa kuti adye?”+ 38 Iye anawafunsa kuti: “Muli ndi mitanda ingati ya mkate? Pitani mukaone!” Ataiona ananena kuti: “Ilipo 5 ndi nsomba ziwiri.”+

  • Luka 9:12, 13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 Komano nthawi inali chakumadzulo. Choncho atumwi 12 aja anabwera kwa iye nʼkunena kuti: “Kuno nʼkopanda anthu ndipo nthawi yatha, auzeni anthuwa kuti anyamuke, apite mʼmidzi ndi mʼmadera ozungulira kuti akapeze malo ogona komanso chakudya choti adye.”+ 13 Koma iye anawayankha kuti: “Inuyo muwapatse chakudya.”+ Iwo anati: “Tilibe chilichonse kupatulapo mitanda ya mkate isanu ndi nsomba ziwiri zokha basi. Kapenatu tipite kukagula chakudya chokwanira anthu onsewa.”

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena