Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Mateyu 10:2
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 2 Mayina a atumwi 12 ndi awa:+ Simoni, amene ankatchulidwa kuti Petulo*+ ndi Andireya+ mchimwene wake. Yakobo mwana wa Zebedayo ndi mchimwene wake Yohane.+

  • Mateyu 10:4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 4 Simoni Kananiya* ndi Yudasi Isikariyoti, amene pambuyo pake anapereka Yesu.+

  • Luka 6:12-16
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 Mʼmasiku amenewo, Yesu anapita kuphiri kukapemphera+ ndipo anachezera usiku wonse kupemphera kwa Mulungu.+ 13 Kutacha, anaitana ophunzira ake nʼkusankhapo 12, amenenso anawapatsa dzina lakuti atumwi.+ 14 Iye anasankha Simoni, amene ankatchulidwa kuti Petulo, ndi Andireya mchimwene wake. Anasankhanso Yakobo, Yohane, Filipo,+ Batolomeyo, 15 Mateyu, Tomasi,+ Yakobo mwana wa Alifeyo, ndi Simoni wotchedwa “wakhama.” 16 Komanso anasankha Yudasi mwana wa Yakobo ndi Yudasi Isikariyoti, amene pambuyo pake anamupereka.

  • Yohane 6:70, 71
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 70 Yesu anawauza kuti: “Ine ndinakusankhani inu 12, si choncho?+ Komatu mmodzi wa inu ndi wonenera anzake zoipa.”*+ 71 Kwenikweni ankanena za Yudasi mwana wa Simoni Isikariyoti, chifukwa ameneyu anali kudzamupereka, ngakhale kuti anali mmodzi wa ophunzira 12 aja.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena