Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Danieli 9:24-27
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 24 Pali milungu* 70 imene yaikidwa yokhudza anthu a mtundu wako ndi mzinda wanu woyera+ ndi cholinga choti athetse kuphwanya malamulo, athetse machimo,+ aphimbe cholakwa,+ abweretse chilungamo kuti chikhalepo mpaka kalekale,+ adinde chidindo pamasomphenya ndi maulosi,*+ ndiponso kuti adzoze Malo Opatulika Koposa.* 25 Uyenera kudziwa ndi kuzindikira kuti kuchokera pamene lamulo lakuti Yerusalemu akonzedwe ndi kumangidwanso+ lidzaperekedwe kukafika pamene Mesiya*+ Mtsogoleri+ adzaonekere, padzadutsa milungu 7 komanso milungu 62.+ Yerusalemu adzakonzedwa ndi kumangidwanso ndipo adzakhala ndi bwalo ndi ngalande yachitetezo. Koma zimenezi zidzachitika pa nthawi ya mavuto.

      26 Pambuyo pa milungu 62 imeneyi, Mesiya adzaphedwa+ ndipo sadzasiya kalikonse.+

      Mtsogoleri adzabwera ndi gulu lake lankhondo ndipo adzawononga mzindawo ndi malo oyera.+ Malo oyerawo adzafafanizidwa ndi madzi osefukira ndipo padzakhala nkhondo mpaka kumapeto. Mogwirizana ndi zimene Mulungu wasankha, kudzakhala chiwonongeko.+

      27 Iye* adzasungira anthu ambiri pangano kwa mlungu umodzi. Ndiye pakatikati pa mlunguwo adzathetsa nsembe zanyama ndi nsembe zina zoperekedwa ngati mphatso.+

      Wowonongayo adzabwera pamapiko a zinthu zonyansa ndipo zimene Mulungu wasankha zija zidzakhuthulidwanso pachowonongedwacho+ kufikira chitafafanizidwa.”

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena