-
Danieli 9:24-27Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
24 Pali milungu* 70 imene yaikidwa yokhudza anthu a mtundu wako ndi mzinda wanu woyera+ ndi cholinga choti athetse kuphwanya malamulo, athetse machimo,+ aphimbe cholakwa,+ abweretse chilungamo kuti chikhalepo mpaka kalekale,+ adinde chidindo pamasomphenya ndi maulosi,*+ ndiponso kuti adzoze Malo Opatulika Koposa.* 25 Uyenera kudziwa ndi kuzindikira kuti kuchokera pamene lamulo lakuti Yerusalemu akonzedwe ndi kumangidwanso+ lidzaperekedwe kukafika pamene Mesiya*+ Mtsogoleri+ adzaonekere, padzadutsa milungu 7 komanso milungu 62.+ Yerusalemu adzakonzedwa ndi kumangidwanso ndipo adzakhala ndi bwalo ndi ngalande yachitetezo. Koma zimenezi zidzachitika pa nthawi ya mavuto.
26 Pambuyo pa milungu 62 imeneyi, Mesiya adzaphedwa+ ndipo sadzasiya kalikonse.+
Mtsogoleri adzabwera ndi gulu lake lankhondo ndipo adzawononga mzindawo ndi malo oyera.+ Malo oyerawo adzafafanizidwa ndi madzi osefukira ndipo padzakhala nkhondo mpaka kumapeto. Mogwirizana ndi zimene Mulungu wasankha, kudzakhala chiwonongeko.+
27 Iye* adzasungira anthu ambiri pangano kwa mlungu umodzi. Ndiye pakatikati pa mlunguwo adzathetsa nsembe zanyama ndi nsembe zina zoperekedwa ngati mphatso.+
Wowonongayo adzabwera pamapiko a zinthu zonyansa ndipo zimene Mulungu wasankha zija zidzakhuthulidwanso pachowonongedwacho+ kufikira chitafafanizidwa.”
-