Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • g99 7/8 tsamba 14
  • Kuda Nkhaŵa Chifukwa cha Magazi Amatenda

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kuda Nkhaŵa Chifukwa cha Magazi Amatenda
  • Galamukani!—1999
  • Nkhani Yofanana
  • Kuthiriridwa Mwazi—Nkwabwino Motani?
    Kodi Mwazi Ungapulumutse Motani Moyo Wanu?
  • Kupulumutsa Moyo ndi Mwazi—Motani?
    Nsanja ya Olonda—1991
  • Kodi Ndimphatso ya Moyo Kapena Mpsopsono wa Imfa?
    Galamukani!—1990
  • Mafunso Ophunzirira Brosha ya Kodi Mwazi Ungapulumutse Motani Moyo Wanu?
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1998
Onani Zambiri
Galamukani!—1999
g99 7/8 tsamba 14

Kuda Nkhaŵa Chifukwa cha Magazi Amatenda

PAMENE Demetrio Pessoa, katswiri wa maphunziro a biochemistry wa ku Bolivia anachitidwa opaleshoni, anadwalanso atangotuluka m’chipatala ndipo mwamsanga anam’tengeranso kuchipatala. Kumeneko anamuika magazi, ndipo anayamba kupezako bwino. Komabe, mosakhalitsa, katswiri wa biochemistry ameneyu anayamba kumva ngati akudwala malungo. Atamuyeza, madokotala anamuuza uthenga womvetsa chisoni: Bamboyu yemwe dzina lake ndi Pessoa anali atalandira magazi amene anali ndi kachilombo kotchedwa Trypanosoma cruzi. Ndiye kuti anatenga matenda otchedwa Chagas.”

Bambo Pessoa si munthu yekhayo amene anakumana ndi zoterezi ku Bolivia, likutero bungwe lofalitsa nkhani la ku London lotchedwa Panos. Kafukufuku wa zachipatala amene anachitidwa kwa nthaŵi yaitali m’mayiko 12 a ku Latin America akusonyeza kuti kumeneko, matenda oyamba chifukwa cha magazi amatenda ndi ofala. M’dziko lina la ku Latin America, mwa odwala 10,000 alionse amene analandira magazi, odwala 220 anatenga matenda opatsirana. Kusonyeza kuti munthu mmodzi mwa anthu 45 alionse anagwidwa ndi matendawo!

Komabe, si matenda a Chagas okhawo amene angatengedwe. Kafukufuku yemweyu akusonyeza kuti mayiko angapo a ku Latin America sankayeza magazi operekedwa ndi anthu kuti aone ngati ali ndi matenda a Hepatitis C ndiponso kuti m’mayiko ena magazi ankayesedwa ngati ali ndi matenda a chindoko mwa kamodzikamodzi basi. Kuphatikizanso apo, mayiko angapo analibe zida zokwanira kuti aziyeza magazi ngati ali ndi HIV. Ponenapo za magazi amatenda, Tonchi Marinkovic, amene ali nduna ya za Umoyo ku Bolivia, ananena kuti: “Mulungu mutiteteze kuti tisathe ndi matenda a chindoko, kutupa chiŵindi, Chagas kapena AIDS kuti asabukenso.”

Ngakhale kuti mwina sichinali cholinga chake, koma munthu woimira boma ameneyu anasonyezadi njira yolondola yothetsera matenda oopsa ameneŵa. Zaka zambiri m’mbuyomu, magazini yotchedwa Notícias Bolivianas inalemba m’nkhani yake ina yonena za kuopsa koika munthu magazi kuti: “Kusala magazi ndiko kovomerezeka mogwirizana ndi lamulo la Baibulo.” Lamulo la Baibulo limene magazini ya ku Bolivia imeneyi ikunena limapezeka pa Machitidwe 15:29. Ndipo limati: “Musale nsembe za mafano, ndi mwazi, ndi zopotola, ndi dama; ngati mudzisungitsa pa zimenezi, kudzakhala bwino kwa inu. Tsalani bwino.”—Onaninso Genesis 9:4; Levitiko 3:17.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena