Ndandanda ya Mlungu wa January 2
MLUNGU WOYAMBIRA JANUARY 2
Nyimbo Na. 17 ndi Pemphero
□ Phunziro la Baibulo la Mpingo:
cf mutu 18 ndime 1-9 (Mph. 25)
□ Sukulu ya Utumiki wa Mulungu:
Kuwerenga Baibulo: Yesaya 24-28 (Mph. 10)
Na. 1: Yesaya 27:1-13 (Osapitirira mph. 4)
Na. 2: Musamakayikire Kuti Yehova Amakukondani—Yes. 57:15 (Mph. 5)
Na. 3: Kodi Cholinga cha Moyo N’chiyani?—rs tsa. 290 ndime 1-tsa. 291 ndime 1 (Mph. 5)
□ Msonkhano wa Utumiki:
Mph. 10: Zilengezo. Pogwiritsa ntchito chitsanzo cha ulaliki chimene chili patsamba lino, chitani chitsanzo chosonyeza mmene mungayambitsire phunziro Loweruka loyamba m’mwezi wa January.
Mph. 10: Zosowa za pampingo.
Mph. 15: Zimene Munganene Pogawira Magazini M’mwezi wa January. Nkhani yokambirana. Kwa mphindi imodzi kapena ziwiri fotokozani nkhani zochepa zimene zili m’magaziniwo zimene zingakhale zothandiza m’gawo la mpingo wanu. Kenako, pogwiritsa ntchito nkhani zoyambirira za mu Nsanja ya Olonda, pemphani omvera kuti anene funso lochititsa chidwi ndiponso lemba limene angawerenge pogawira magaziniwo. Chitaninso chimodzimodzi ndi nkhani zoyambirira m’magazini ya Galamukani! Ngati nthawi ilipo mungachitenso zimenezi ndi nkhani imodzi m’magazini ya Nsanja ya Olonda kapena Galamukani! Limbikitsani ofalitsa kuti ayesetse kugawira magazini a Galamukani! kumalo antchito ndi amalonda. Pemphani woyang’anira utumiki kuti afotokoze zimene zakonzedwa pa ntchito yolalikira m’magawo amenewa. Chitani chitsanzo chosonyeza mmene mungagawirire magazini iliyonse. Pochita chitsanzo chogawira magazini ya Galamukani! sonyezani zimene tingachite polalikira kumalo antchito ndi amalonda.
Nyimbo Na. 86 ndi Pemphero