MAY 12-18
MIYAMBO 13
Nyimbo Na. 34 ndi Pemphero | Mawu Oyamba (1 min.)
1. Musamapusitsike ndi “Nyale ya Anthu Oipa”
(10 min.)
Anthu oipa alibe tsogolo (Miy 13:9; it-2 196 ¶2-3)
Musamachite zinthu ndi anthu amene amaona kuti zoipa n’zabwino (Miy 13:20; w12 7/15 12 ¶3)
Yehova amadalitsa anthu olungama (Miy 13:25; w04 7/15 31 ¶6)
Moyo wa anthu amene amafuna kusangalala ndi dzikoli, si wosangalatsa ngati mmene zimaonekera. Anthu amene amachita zimene Yehova amafuna ndi amene amasangalaladi ndi moyo
2. Mfundo Zothandiza
(10 min.)
Miy 13:24—Kodi lembali likutichenjeza chiyani pa nkhani ya chikondi chosayenera? (it-2 276 ¶2)
Kodi ndi mfundo ziti zimene mwapeza pa kuwerenga Baibulo kwa mlungu uno?
3. Kuwerenga Baibulo
(4 min.) Miy 13:1-17 (th phunziro 10)
4. Ulendo Woyamba
(3 min.) KUNYUMBA NDI NYUMBA. Pambuyo pokambirana nkhani imene yangochitika kumene, werengani naye lemba limene lingamusangalatse. (lmd phunziro 2 mfundo 5)
5. Ulendo Woyamba
(4 min.) KULALIKIRA MWAMWAYI. Muitanireni kumisonkhano yathu. (lmd phunziro 2 mfundo 3)
6. Nkhani
(5 min.) lmd zakumapeto A mfundo 9—Mutu: Ana Omwe Amalemekeza ndi Kumvera Makolo Awo Zinthu Zimawayendera Bwino. (th phunziro 16)
Nyimbo Na. 77
7. “Kuwala kwa Nyale ya Anthu Olungama Kukuwonjezeka Kwambiri”
(8 min.) Nkhani yokambirana.
M’Mawu a Mulungu muli malangizo anzeru kwambiri. Tikamadalira Mawu a Mulungu kuti azititsogolera, zinthu zimatiyendera bwino ndipo timakhala osangalala. Zimenezi sitingazipeze kulikonse m’dzikoli.
Onerani VIDIYO yakuti Dziko Silingakupatse Zinthu Zimene Lilibe. Kenako funsani funso lotsatirali:
Kodi zimene zinachitikira Mlongo Gainanshina zikusonyeza bwanji kuti “nyale ya anthu olungama” imaposa “nyale ya anthu oipa”?—Miy 13:9
Musamataye nthawi yanu ndi kuganizira zinthu zam’dzikoli kapena kunong’oneza bondo chifukwa cha zimene munasankha n’cholinga choti mutumikire Yehova. (1Yo 2:15-17) M’malomwake, muziganizira ‘zinthu zamtengo wapatali’ zimene munapeza.—Afi 3:8.
8. Zofunika Pampingo
(7 min.)
9. Phunziro la Baibulo la Mpingo
(30 min.) bt mutu 26 ¶9-17