Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb25 May tsamba 4-5
  • May 12-18

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • May 12-18
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Kabuku ka Msonkhano—2025
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Kabuku ka Msonkhano—2025
mwb25 May tsamba 4-5

MAY 12-18

MIYAMBO 13

Nyimbo Na. 34 ndi Pemphero | Mawu Oyamba (1 min.)

CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

1. Musamapusitsike ndi “Nyale ya Anthu Oipa”

(10 min.)

Anthu oipa alibe tsogolo (Miy 13:9; it-2 196 ¶2-3)

Musamachite zinthu ndi anthu amene amaona kuti zoipa n’zabwino (Miy 13:20; w12 7/15 12 ¶3)

Yehova amadalitsa anthu olungama (Miy 13:25; w04 7/15 31 ¶6)

Zithunzi zosonyeza zinthu zoipa zimene munthu amene si wa Mboni akuchita, ndi zinthu zabwino zimene anthu a Mboni akuchita. 1. Mnyamata ali ku bala ndipo akuvina atanyamula kapu ya chakumwa m’manja. 2. Kenako wadwala ndipo akumwa mankhwala. 3. Abale ndi alongo akucheza panja chakumadzulo. A Mboni aja akuimba nyimbo, kuvina komanso kudya mosangalala. 4. Tsiku lotsatira, abale aja akulalikira.

Moyo wa anthu amene amafuna kusangalala ndi dzikoli, si wosangalatsa ngati mmene zimaonekera. Anthu amene amachita zimene Yehova amafuna ndi amene amasangalaladi ndi moyo

2. Mfundo Zothandiza

(10 min.)

  • Miy 13:24—Kodi lembali likutichenjeza chiyani pa nkhani ya chikondi chosayenera? (it-2 276 ¶2)

  • Kodi ndi mfundo ziti zimene mwapeza pa kuwerenga Baibulo kwa mlungu uno?

3. Kuwerenga Baibulo

(4 min.) Miy 13:1-17 (th phunziro 10)

KUPHUNZITSA MWALUSO MU UTUMIKI

4. Ulendo Woyamba

(3 min.) KUNYUMBA NDI NYUMBA. Pambuyo pokambirana nkhani imene yangochitika kumene, werengani naye lemba limene lingamusangalatse. (lmd phunziro 2 mfundo 5)

5. Ulendo Woyamba

(4 min.) KULALIKIRA MWAMWAYI. Muitanireni kumisonkhano yathu. (lmd phunziro 2 mfundo 3)

6. Nkhani

(5 min.) lmd zakumapeto A mfundo 9—Mutu: Ana Omwe Amalemekeza ndi Kumvera Makolo Awo Zinthu Zimawayendera Bwino. (th phunziro 16)

MOYO WATHU WA CHIKHRISTU

Nyimbo Na. 77

7. “Kuwala kwa Nyale ya Anthu Olungama Kukuwonjezeka Kwambiri”

(8 min.) Nkhani yokambirana.

M’Mawu a Mulungu muli malangizo anzeru kwambiri. Tikamadalira Mawu a Mulungu kuti azititsogolera, zinthu zimatiyendera bwino ndipo timakhala osangalala. Zimenezi sitingazipeze kulikonse m’dzikoli.

Chithunzi cha muvidiyo yakuti Dziko “Silingakupatse Zinthu Zimene Lilibe.” Mlongo Gainanshina wakhala m’munda wa maluwa ndipo akuyang’ana kumwamba.

Onerani VIDIYO yakuti Dziko Silingakupatse Zinthu Zimene Lilibe. Kenako funsani funso lotsatirali:

  • Kodi zimene zinachitikira Mlongo Gainanshina zikusonyeza bwanji kuti “nyale ya anthu olungama” imaposa “nyale ya anthu oipa”?—Miy 13:9

Musamataye nthawi yanu ndi kuganizira zinthu zam’dzikoli kapena kunong’oneza bondo chifukwa cha zimene munasankha n’cholinga choti mutumikire Yehova. (1Yo 2:15-17) M’malomwake, muziganizira ‘zinthu zamtengo wapatali’ zimene munapeza.—Afi 3:8.

ZOMWE MUNGACHITE PA KULAMBIRA KWA PABANJA:

Nthawi ndi nthawi, muzionera vidiyo imodzi kapena mavidiyo awiri opezeka pa mavidiyo a mutu wakuti Mfundo za m’Baibulo Zimasintha Anthu. Muziganizira mmene mavidiyowa amafotokozera kufunika kwa choonadi.

8. Zofunika Pampingo

(7 min.)

9. Phunziro la Baibulo la Mpingo

(30 min.) bt mutu 26 ¶9-17

Mawu Omaliza (3 min.) | Nyimbo Na. 43 ndi Pemphero

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena