Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb25 September tsamba 12-13
  • October 13-19

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • October 13-19
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Kabuku ka Msonkhano—2025
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Kabuku ka Msonkhano—2025
mwb25 September tsamba 12-13

OCTOBER 13-19

MLALIKI 7-8

Nyimbo Na. 39 ndi Pemphero | Mawu Oyamba (1 min.)

CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

1. ‘Muzipita Kunyumba Yamaliro’

(10 min.)

Muzipeza nthawi yotonthoza anthu amene akulira (Mla 7:2; it “Kulira” ¶9)

Muzitonthoza anthu amene aferedwa powauza zinthu zabwino zimene womwalirayo ankachita (Mla 7:1; w19.06 23 ¶15)

Muzipemphera ndi anthu amene akulira (w17.07 16 ¶16)

Banja likucheza ndi m’bale amene mkazi wake anamwalira. Akuona zithunzi zosonyeza zinthu zosangalatsa zomwe ankachitira limodzi.

KUMBUKIRANI: Anthu amene okondedwa awo amwalira, nthawi zambiri amafunikabe kuthandizidwa ndi Akhristu anzawo kwa nthawi ndithu pambuyo pa imfayo.—w17.07 16 ¶17-19.

2. Mfundo Zothandiza

(10 min.)

  • Mla 7:20-22—Kodi mavesiwa angatithandize bwanji kudziwa ngati tikuyenera kufunsa munthu amene watinenera zoipa? (w23.03 31 ¶18)

  • Kodi ndi mfundo ziti zimene mwapeza pa kuwerenga Baibulo kwa mlungu uno?

3. Kuwerenga Baibulo

(4 min.) Mla 8:1-13 (th phunziro 10)

KUPHUNZITSA MWALUSO MU UTUMIKI

4. Ulendo Woyamba

(2 min.) KULALIKIRA M’MALO OPEZEKA ANTHU AMBIRI. Pezani nkhani yomwe ingasangalatse munthuyo ndipo konzani zoti mudzakumanenso. (lmd phunziro 2 mfundo 4)

5. Ulendo Woyamba

(2 min.) KULALIKIRA MWAMWAYI. (lmd phunziro 2 mfundo 3)

6. Ulendo Wobwereza

(2 min.) KUNYUMBA NDI NYUMBA. Muonetseni chimodzi mwa zinthu zopezeka pa webusaiti yathu ya jw.org. (lmd phunziro 9 mfundo 4)

7. Kufotokoza Zimene Mumakhulupirira

(5 min.) Chitsanzo. ijwfq nkhani na. 50—Mutu: Kodi N’chiyani Chimachitika pa Maliro a Mboni za Yehova? (th phunziro 17)

MOYO WATHU WA CHIKHRISTU

Nyimbo Na. 151

8. Muzilimbitsa Chikhulupiriro Chanu Choti Akufa Adzauka

(15 min.) Nkhani yokambirana.

Chithunzi cha muvidiyo yakuti “Tsanzirani Akazi a Chikhulupiriro Cholimba​—⁠Marita.” Marita ndi Mariya akusangalala kulandira Lazaro yemwe waukitsidwa.

Lonjezo la Yehova lakuti akufa adzauka ndi limodzi mwa malonjezo a mtengo wapatali kwambiri kwa ife. Limatiphunzitsa za makhalidwe ake abwino monga, mphamvu, nzeru, chifundo komanso chikondi chimene amasonyeza aliyense payekha.—Yoh 3:16.

Tikamakhulupirira kwambiri kuti akufa adzauka, sitimadera nkhawa kwambiri za mavuto amene tikukumana nawo. (2Ak 4:16-18) Chiyembekezo chimenechi chingatipatsenso mtendere komanso kutilimbikitsa pamene tikuzunzidwa, tikudwala kapena pamene wokondedwa wathu wamwalira. (1At 4:13) Sitingamasangalale ngati sitikhulupirira kuti akufa adzauka. (1Ak 15:19) Ndiye nthawi zonse muziyesetsa kulimbitsa chikhulupiriro chanu chimenechi.

Werengani Yohane 11:21-24. Kenako funsani mafunso awa:

  • Kodi Marita anasonyeza bwanji kuti ankakhulupirira kwambiri kuti akufa adzauka?

  • Kodi anadalitsidwa bwanji chifukwa cha chikhulupiriro chakechi?—Yoh 11:38-44

Onerani VIDIYO yakuti Tsanzirani Akazi a Chikhulupiriro Cholimba—Marita. Kenako funsani mafunso awa:

  • N’chifukwa chiyani chiyembekezo chakuti akufa adzauka n’chofunika kwambiri kwa inu?

  • Kodi mungatani kuti chikhulupiriro chanu chakuti akufa adzauka chikhalebe cholimba kwambiri?

9. Phunziro la Baibulo la Mpingo

(30 min.) lfb mutu 26-27

Mawu Omaliza (3 min.) | Nyimbo Na. 124 ndi Pemphero

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena