Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb25 September tsamba 10-11
  • October 6-12

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • October 6-12
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Kabuku ka Msonkhano—2025
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Kabuku ka Msonkhano—2025
mwb25 September tsamba 10-11

OCTOBER 6-12

MLALIKI 5-6

Nyimbo Na. 42 ndi Pemphero | Mawu Oyamba (1 min.)

CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

Aisiraeli omwe ali pageti akumvetsera pamene wansembe akulankhula. Wansembeyo wanyamula mpukutu.

Aisiraeli akumvetsera mwatcheru pamene wansembe akufotokoza Chilamulo

1. Kodi Timasonyeza Bwanji Kuti Timalemekeza Mulungu Wathu Wamkulu?

(10 min.)

Tingasonyeze ulemu pamisonkhano tikamamvetsera komanso tikamavala ndi kudzikongoletsa moyenera (Mla 5:1; w08 8/15 15-16 ¶17-18)

Tikamapereka mapemphero a pagulu omwe si aatali komanso omwe ndi aulemu (Mla 5:2; w09 11/15 11 ¶21)

Tikamasungabe lonjezo lathu loti tidzatumikira Yehova (Mla 5:4-6; w17.04 6 ¶12)

Abale ndi alongo amisinkhu yosiyanasiyana akumvetsera mwatcheru pamisonkhano m’Nyumba ya Ufumu.

2. Mfundo Zothandiza

(10 min.)

  • Mla 5:8—Kodi lembali lingatilimbikitse bwanji ngati tachitiridwa zinthu zopanda chilungamo? (w20.09 31 ¶3-5)

  • Kodi ndi mfundo ziti zimene mwapeza pa kuwerenga Baibulo kwa mlungu uno?

3. Kuwerenga Baibulo

(4 min.) Mla 5:1-17 (th phunziro 12)

KUPHUNZITSA MWALUSO MU UTUMIKI

4. Ulendo Woyamba

(1 min.) KUNYUMBA NDI NYUMBA. Munthuyo akufuna kukangana nanu. (lmd phunziro 4 mfundo 5)

5. Ulendo Woyamba

(2 min.) KULALIKIRA M’MALO OPEZEKA ANTHU AMBIRI. Kambiranani nkhani imodzi yopezeka pagawo lakuti “Choonadi Chomwe Timakonda Kuphunzitsa Anthu” mu zakumapeto A, m’kabuku kakuti Muzikonda Anthu—Muziwaphunzitsa. (lmd phunziro 1 mfundo 3)

6. Ulendo Wobwereza

(3 min.) KUNYUMBA NDI NYUMBA. Gwiritsani ntchito vidiyo yopezeka pa Zinthu Zophunzitsira. (lmd phunziro 7 mfundo 3)

7. Kuphunzitsa Anthu

(5 min.) lff phunziro 17 mawu oyamba komanso mfundo 1-3 (lmd phunziro 11 mfundo 3)

MOYO WATHU WA CHIKHRISTU

Nyimbo Na. 160

8. Kodi Mumagwiritsa Ntchito Gawo Lakuti “Choonadi Chomwe Timakonda Kuphunzitsa Anthu”?

(15 min.) Nkhani yokambirana.

Banja likulalikira nyumba ndi nyumba likuwerengera mnyamata Baibulo.

Kungoyambira nthawi imene kabuku kakuti Muzikonda Anthu—Muziwaphunzitsa kanatuluka, kakhala kakutithandiza kuti tiwonjezere maluso athu pokambirana ndi anthu. Zakumapeto A m’kabukuka, zinakonzedwa kuti zizitithandiza kuyamba kukambirana ndi anthu mfundo zosavuta kumva za choonadi cha m’Baibulo. (Ahe 4:12) Kodi mumadziwa bwino nkhani zonse 9 zomwe zimapezeka pagawo lakuti “Choonadi Chomwe Timakonda Kuphunzitsa Anthu”?

  • Kodi tingayambe bwanji kukambirana ndi anthu mfundo yosavuta kumva ya choonadi cha m’Baibulo pamene tikucheza?—lmd zakumapeto A

  • Kodi ndi nkhani ziti zimene mwaona kuti ndi zothandiza kwambiri m’gawo lanu?

  • Kodi mungatani kuti mudziwe bwino malemba omwe ali mu zakumapeto A?

CHOLINGA:

Muziyesetsa kukumbukira ngakhale lemba limodzi lokha pa nkhani iliyonse mu zakumapeto A. Muziyamba ndi malemba a nkhani zimene zimachititsa chidwi kwambiri anthu m’gawo lanu.

Tikamagwiritsa ntchito malembawa kawirikawiri mu utumiki, m’pamenenso tingawadziwe bwino kwambiri. Koma kuti tizitha kuwagwiritsa ntchito, choyamba tiyenera kuzolowera kulankhulana ndi anthu a m’dera lathu.

Onerani VIDIYO yakuti “Chitsulo Chimanola Chitsulo Chinzake”—Kulalikira Anthu Ambiri. Kenako funsani funso ili:

  • Kodi n’chiyani chingatithandize kuti tizilankhula ndi anthu ambiri m’gawo lathu?

9. Phunziro la Baibulo la Mpingo

(30 min.) lfb mutu 24-25

Mawu Omaliza (3 min.) | Nyimbo Na. 34 ndi Pemphero

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena