Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb25 November tsamba 6-7
  • November 17-23

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • November 17-23
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Kabuku ka Msonkhano—2025
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Kabuku ka Msonkhano—2025
mwb25 November tsamba 6-7

NOVEMBER 17-23

NYIMBO YA SOLOMO 6-8

Nyimbo Na. 34 ndi Pemphero | Mawu Oyamba (1 min.)

CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

1. Muzikhala Khoma, Osati Chitseko

(10 min.)

Azichimwene ake a Msulami ankafuna kuti iye asagonane ndi mwamuna aliyense asanalowe m’banja (Nym 8:8, 9; it “Nyimbo ya Solomo” ¶11)

Iye anapeza mtendere chifukwa anayesetsa kupeweratu makhalidwe oipa (Nym 8:​10; yp 188 ¶2)

Iye ndi chitsanzo chabwino kwambiri kwa achinyamata pa nkhani imeneyi (yp2 33)

Amuna atatu a Chiisiraeli aima kutsogolo kwa khoma lamiyala ndipo apinda manja.

DZIFUNSENI KUTI, ‘Kodi ndingathandize bwanji Akhristu omwe sali pabanja mumpingo wathu kuti akhale khoma osati chitseko?’

2. Mfundo Zothandiza

(10 min.)

  • Nym 8:6—N’chifukwa chiyani chikondi chenicheni chimatchulidwanso kuti “lawi la Ya”? (w15 1/15 29 ¶3)

  • Kodi ndi mfundo ziti zimene mwapeza pa kuwerenga Baibulo kwa mlungu uno?

3. Kuwerenga Baibulo

(4 min.) Nym 7:1-13 (th phunziro 12)

KUPHUNZITSA MWALUSO MU UTUMIKI

4. Ulendo Woyamba

(2 min.)KUNYUMBA NDI NYUMBA. Gwiritsani ntchito khadi lodziwitsa anthu za jw.org kuti muyambe kukambirana ndi munthu. (lmd phunziro 4 mfundo 4)

5. Ulendo Woyamba

(2 min.) KULALIKIRA M’MALO OPEZEKA ANTHU AMBIRI. Gwiritsani ntchito kapepala kuti muyambe kukambirana ndi munthu kumaofesi kapena malo ena ogwirira ntchito. (lmd phunziro 1 mfundo 4)

6. Ulendo Woyamba

(2 min.) KULALIKIRA MWAMWAYI. Yambani kucheza ndi munthu, koma machezawo athe musanamulalikire. (lmd phunziro 2 mfundo 4)

7. Kufotokoza Zimene Mumakhulupirira

(5 min.) Chitsanzo. ijwfq nkhani Na. 43—Mutu: Kodi a Mboni za Yehova Amatsatira Mfundo Ziti Zokhudza Kukhala pa Chibwenzi? (th phunziro 7)

MOYO WATHU WA CHIKHRISTU

Nyimbo Na. 121

8. Thawani Chiwerewere

(15 min.) Nkhani yokambirana.

M’buku la Nyimbo ya Solomo, m’busa anaitana Msulami kuti akayende naye ngati njira yosonyezerana chikondi. (Nym 2:​10-​14) Ngakhale kuti m’busayo analibe zolinga zoipa, azichimwene ake a Msulami, mwanzeru, anamupatsa ntchito zoti agwire n’cholinga choti asapite kokayendako. (Nym 2:​15) Azichimwene akewo ankadziwa kuti anthu amene amakondana akakhala awiriwiri, akhoza kuyesedwa kuti achite tchimo.

Baibulo limauza Akhristu kuti ‘athawe chiwerewere.’ (1Ak 6:18) Tiyenera kupewa chilichonse chomwe chingatichititse kuti tichite tchimo. Amene analemba buku la Nyimbo ya Solomo, anauziridwanso kulemba kuti: “Munthu wochenjera akaona tsoka amabisala, koma wosadziwa zinthu amangopitabe ndipo amakumana ndi mavuto.”—Miy 22:3.

Onerani VIDIYO yakuti Mulungu “Amadziwa Zinsinsi za Mumtima.” Kenako funsani funso ili:

  • Kodi mwaphunzira chiyani muvidiyoyi?

    Zithunzi za muvidiyo yakuti Mulungu “Amadziwa Zinsinsi za Mumtima.” M’bale walandira meseji pa nthawi ya misonkhano.
    Zithunzi za muvidiyo yakuti Mulungu “Amadziwa Zinsinsi za Mumtima.” M’bale wakhala pafupi ndi mtsikana kusukulu ndipo mtsikanayo akumugwira dzanja.
    Zithunzi za muvidiyo yakuti Mulungu “Amadziwa Zinsinsi za Mumtima.” M’bale akulankhula ndi makolo ake pa nthawi imene akudya.

9. Phunziro la Baibulo la Mpingo

(30 min.) lfb mutu 36-37

Mawu Omaliza (3 min.) | Nyimbo Na. 51 ndi Pemphero

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena