Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb25 November tsamba 10-11
  • December 8-14

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • December 8-14
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Kabuku ka Msonkhano—2025
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Kabuku ka Msonkhano—2025
mwb25 November tsamba 10-11

DECEMBER 8-14

YESAYA 6-8

Nyimbo Na. 75 ndi Pemphero | Mawu Oyamba (1 min.)

CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU

Yesaya akuyang’ana kumwamba ndipo akudzipereka kuti akhale mneneri wa Mulungu.

1. “Ine Ndilipo! Nditumizeni”

(10 min.)

Popanda kuzengereza, Yesaya anadzipereka kuti akhale mneneri wa Mulungu (Yes 6:8; ip-1 93-94 ¶13-14)

Utumiki wa Yesaya unali woti udzakhala wovuta (Yes 6:9, 10; ip-1 95 ¶15-16)

Utumiki wa Yesaya unkasonyeza ntchito imene Yesu adzagwire (Mt 13:​13-15; ip-1 99 ¶23)

Yesaya akuuza gulu la anthu omwe ali pamsika uthenga wochokera kwa Yehova. Aisiraeli ena sakumvetsera pomwe ena akuchokapo atakwiya.

FUNSO LOFUNIKA KULIGANIZIRA: Kodi ndingasinthe zinthu ziti kuti ndizichita zambiri potumikira Yehova?

2. Mfundo Zothandiza

(10 min.)

  • Yes 7:3, 4—N’chifukwa chiyani Yehova anapulumutsa Ahazi, yemwe anali mfumu yoipa? (w06 12/1 9 ¶4)

  • Kodi ndi mfundo ziti zimene mwapeza pa kuwerenga Baibulo kwa mlungu uno?

3. Kuwerenga Baibulo

(4 min.) Yes 8:​1-13 (th phunziro 5)

KUPHUNZITSA MWALUSO MU UTUMIKI

4. Ulendo Woyamba

(3 min.) KUNYUMBA NDI NYUMBA. Kambiranani mfundo imodzi ya choonadi yopezeka mu zakumapeto A, m’kabuku kakuti Muzikonda Anthu. (lmd phunziro 4 mfundo 5)

5. Ulendo Wobwereza

(4 min.) KUNYUMBA NDI NYUMBA. M’pempheni kuti muziphunzira naye Baibulo. (lmd phunziro 9 mfundo 3)

6. Ulendo Wobwereza

(5 min.) KUNYUMBA NDI NYUMBA. Musonyezeni mmene phunziro la Baibulo limachitikira. (lmd phunziro 9 mfundo 5)

MOYO WATHU WA CHIKHRISTU

Nyimbo Na. 83

7. Timadziwika ndi Ntchito Yolalikira Kunyumba ndi Nyumba

(15 min.) Nkhani yokambirana.

A Mboni za Yehova amadziwika ndi ntchito yolalikira kunyumba ndi nyumba, yomwe amaigwira potsanzira Yesu Khristu komanso Akhristu a m’nthawi ya atumwi.—Lu 10:5; Mac 5:42.

N’zoona kuti ntchito yolalikira kunyumba ndi nyumba inaimitsidwa kaye pa nthawi ya mliri wa COVID-19. Choncho tinkauza ena uthenga wabwino polalikira mwamwayi, polemba makalata komanso poimba mafoni. Timasangalala kwambiri kuti tinali ndi mwayi wodziwa bwino njira zolalikirira zimenezi. Komabe, kulalikira kunyumba ndi nyumba idakali njira yaikulu yolalikirira uthenga wabwino. Kodi mumakwanitsa kugwira nawo ntchito yolalikira kunyumba ndi nyumba nthawi zonse?

Kodi kulalikira kunyumba ndi nyumba kumatithandiza bwanji kuchita zinthu zotsatirazi?

  • Kulalikira gawo lathu lonse

  • Kukulitsa luso lathu lophunzitsa komanso kukulitsa makhalidwe abwino monga kulimba mtima, kupanda tsankho komanso kudzipereka

  • Kuyambitsa maphunziro a Baibulo

Chithunzi cha muvidiyo yakuti “Timalalikira M’nyengo Iliyonse.” Alongo awiri akulalikira mayi wina panyumba yake.

Onerani VIDIYO yakuti Timalalikira M’nyengo Iliyonse. Kenako funsani funso ili:

  • Kodi mwaphunzira chiyani pa kudzipereka kwa abale ndi alongo amene ankalalikira kuzilumba za Faroe?

8. Phunziro la Baibulo la Mpingo

(30 min.) lfb mutu 42-43

Mawu Omaliza (3 min.) | Nyimbo Na. 123 ndi Pemphero

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena