Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w23 April tsamba 32
  • Mungaphunzirenso Izi

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mungaphunzirenso Izi
  • Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2023
  • Timitu
  • Nkhani Yofanana
  • Kodi mumapindula ndi malifalensi ofotokoza mavesi a m’Baibulo, opezeka mu Buku la Mboni za Yehova Lofufuzira Nkhani?
  • Kodi Mumagwiritsa Ntchito Laibulale ya JW?
    Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2016
  • Buku Lothandiza Kufufuza Nkhani
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2014
  • Mfundo Zothandiza Pophunzira
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2023
  • Muzigwiritsa Ntchito Zinthu Zofufuzira
    Kabuku ka Msonkhano wa Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2021
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2023
w23 April tsamba 32

Mungaphunzirenso Izi

Kodi mumapindula ndi malifalensi ofotokoza mavesi a m’Baibulo, opezeka mu Buku la Mboni za Yehova Lofufuzira Nkhani?

Malifalensi ofotokozera malembawa angakuthandizeni kuti muzifufuza mozama Mawu a Mulungu. Malifalensiwa angakhale ofotokoza mmene zinthu zinalili pamene zinthu zomwe zalembedwa pa vesi linalake zinkachitika, chifukwa chake vesilo linalembedwa, amene ankakhudzidwa ndi zinthu zofotokozedwa palembalo kapenanso tanthauzo lenileni la mawu ena ake.

Pa LAIBULALE YA PA INTANETI komanso pa JW Library, mungathe kupeza malifalensi a m’Buku Lofufuzira Nkhani mwachindunji pa mavesi a m’Baibulo. Mungapeze malifalensiwa m’Mabaibulo amene muli nawo pachipangizo chanu.

Mukamagwiritsa ntchito malifalensiwa muziyang’anitsitsa madeti ake. Nkhani zatsopano zimakhala pamwamba. Mukamatsika m’munsi mungapeze nkhani zakale zomwe mwina panopa mfundo zake zinasintha kamvedwe.

  • Pa LAIBULALE YA PA INTANETI malifalensiwa amapezeka mukangodina vesilo.

  • Kuti mupeze malifalensi a mavesi a m’Baibulo pa JW Library, muyenera kupanga dawunilodi Buku Lofufuzira Nkhani ndipo muzilipanganso dawunilodi mukaikidwa zinthu zatsopano. Mungachite zimenezi podina pamene alemba kuti “Download” pakagawo kophunzirira mukangotsegula chaputala cha Baibulo.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena