Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • km 8/07 tsamba 1
  • Kulambira Yehova Pamodzi Monga Banja

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Kulambira Yehova Pamodzi Monga Banja
  • Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
  • Nkhani Yofanana
  • Banja Lachikristu Limachitira Zinthu Pamodzi
    Nsanja ya Olonda—1993
  • Mphatso Yothandiza kwa Mabanja
    Utumiki Wathu wa Ufumu—2011
  • Mmene Banja Limachitira Zinthu Pamodzi Kuti Onse Azitengamo Mbali Mokwanira—Mu Utumiki
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1999
  • Kumanga Banja Lolimba Mwauzimu
    Nsanja ya Olonda—2001
Onani Zambiri
Utumiki Wathu wa Ufumu—2007
km 8/07 tsamba 1

Kulambira Yehova Pamodzi Monga Banja

1 M’nthawi za m’Baibulo, anthu pabanja ankachitira pamodzi zinthu zambiri. Ankachitira limodzi ntchito zapakhomo koma chofunika kwambiri chinali chakuti ankalambira Yehova monga banja. (Lev. 10:12-14; Deut. 31:12) Masiku ano, m’madera ambiri, ndi zinthu zochepa zomwe anthu pabanja amachitira limodzi. Koma Akhristu amaona kuti kuchita zinthu pamodzi monga banja n’kofunika, makamaka pankhani yolambira. Yehova yemwe anayambitsa banja amasangalala kwambiri akamaona mabanja akum’lambira pamodzi mogwirizana.

2 Lalikirani Pamodzi: Banja limakhala logwirizana kwambiri likamagwirira pamodzi ntchito yolalikira uthenga wabwino. Motero, kuwonjezera pa kugwira ntchito yolalikira ndi anthu ena mumpingo, mkulu afunikiranso kumayenda mokhazikika ndi mkazi wake ndiponso ana ake. (1 Tim. 3:4, 5) Ngakhale kuti oyang’anira oyendayenda amakhala otanganidwa kwambiri, iwo amapatula nthawi yoyenda ndi akazi awo muutumiki.

3 Makolo amene amalalikira limodzi ndi ana awo amatha kuwathandiza kuti akhale aluso polengeza uthenga wabwino. Kuwonjezera pa kuona chimwemwe chimene makolo awo amakhala nacho muutumiki, ana adzaonanso mmene makolowo amakondera Yehova ndiponso anthu ena. (Deut. 6:5-7) Ngakhale anawo atakula zimenezi n’zofunikabe. Mwamuna wina ndi mkazi wake omwe ali ndi ana amuna atatu azaka za pakati pa 15 ndi 21 amayendabe limodzi ndi anawo muutumiki nthawi ndi nthawi. Bamboyo anati: “Nthawi zonse timawaphunzitsa kenakake. Ndipo timaonetsetsa kuti asangalale ndi kulimbikitsidwa.”

4 Konzekerani Pamodzi: Mabanja aona kuti n’kopindulitsa kukonzekera pamodzi utumiki wa kumunda. Nthawi zambiri ana amasangalala pamene m’banja muyeserera utumiki mukumasinthanasinthana kulalikira kapena kukhala mwininyumba. Mabanja ena amagwiritsa ntchito mphindi zomalizira za phunziro lawo labanja kuti achite zimenezi.

5 Chimwemwe chathu chimawonjezereka tikamagwira ntchito zofunika ndiponso zosangalatsa pamodzi ndi anthu amene timawakonda. Anthu m’banja amasangalala kwambiri akamachitira pamodzi utumiki wolalikira nyumba ndi nyumba, kupanga maulendo obwereza ndiponso kuchititsa maphunziro a Baibulo. Motero, mukamalambira Yehova pamodzi ndi banja lanu, munganene mosangalala kuti: ‘Ine, ndi a m’nyumba yanga, tizitumikira Yehova.’—Yos. 24:15.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena