Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb20 October tsamba 8
  • Tidzagwira Ntchito Yapadera mu November Yolengeza za Ufumu wa Mulungu

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Tidzagwira Ntchito Yapadera mu November Yolengeza za Ufumu wa Mulungu
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2020
  • Nkhani Yofanana
  • Ntchito Yapadera Yolengeza za Ufumu wa Mulungu mu September
    Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2023
  • Muzilalikira Uthenga Wabwino Wakuti Dziko Labwino Layandikira
    Kabuku ka Msonkhano wa Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—2021
  • Zimene Tinganene mu Utumiki
    Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2020
  • Gaŵirani Uthenga wa Ufumu Na. 35 Kulikonse
    Utumiki Wathu wa Ufumu—1997
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu Wachikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2020
mwb20 October tsamba 8
M’bale ndi mlongo akulalikira pogwiritsa ntchito mashelefu ndipo akulankhula ndi anthu. Pa shelefu imodzi pali ‘Nsanja ya Olonda’ Na. 2 2020.

MOYO WATHU WACHIKHRISTU

Tidzagwira Ntchito Yapadera mu November Yolengeza za Ufumu wa Mulungu

‘Nsanja ya Olonda’ Na. 2 2020 ya mutu wakuti ‘Kodi Ufumu wa Mulungu N’chiyani?’

Yesu analengeza “uthenga wabwino wa ufumu wa Mulungu.” (Lu 4:43) Iye anaphunzitsanso anthu kuti azipemphera kuti Ufumuwo ubwere. (Mt 6:9, 10) M’mwezi wa November tizidzayesetsa kulengeza kwambiri za Ufumu wa Mulungu. (Mt 24:14) Mukonze zinthu n’cholinga choti mudzathe kugwira nawo mwakhama ntchito imeneyi. Onse amene adzachite upainiya wothandiza adzatha kusankha kupereka maola 30 kapena 50 pa mwezi umenewu.

Tizidzayesetsa kuwerengera anthu ambiri m’gawo lathu lemba lokhudza Ufumu wa Mulungu. Mukamadzasankha lemba loti muwerenge, muzidzaganizira za chipembedzo cha anthuwo. Munthu akadzasonyeza chidwi, mudzamugawire Nsanja ya Olonda Na. 2 2020. Kenako musadzachedwe kupitanso kwa munthuyo n’cholinga choti mudzayambe kuphunzira naye Baibulo pogwiritsa ntchito chimodzi mwa Zinthu Zophunzitsira. Nthawi yoti Ufumu wa Mulungu uwononge maboma onse otsutsa Ufumuwo yayandikira kwambiri. (Da 2:44; 1Ak 15:24, 25) Choncho tiyeni tidzayesetse kugwira nawo mwakhama ntchito yapaderayi kuti tisonyeze kuti ndife okhulupirika kwa Yehova komanso Ufumu wake.

Yesu wakhala pampando wake wachifumu kumwamba ndipo akulamulira dziko lapansi latsopano monga Mfumu.

Ufumu wa Mulungu Udzabweretsa madalitso ambiri padzikoli!

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena