8 Patapita nthawi, Farao anaitana Mose ndi Aroni ndi kuwauza kuti: “Chondererani Yehova+ kuti achotse achule pa ine ndi anthu anga, pakuti ndikufuna kulola anthu anu kuti apite kukapereka nsembe kwa Yehova.”+
19 Zitatero, anthu onse anayamba kuuza Samueli kuti: “Pempherera+ atumiki ako kwa Yehova Mulungu wako, chifukwa sitikufuna kufa. Pakuti tawonjeza choipa china pa machimo athu onse, mwa kupempha kuti tikhale ndi mfumu.”