Yesaya
13 Uwu ndi uthenga wokhudza Babulo,+ umene Yesaya mwana wa Amozi+ anaona m’masomphenya: 2 “Amuna inu, imikani chizindikiro+ paphiri la miyala yokhayokha. Afuulireni! Akodoleni ndi dzanja,+ kuti adzalowe pamakomo a anthu olemekezeka.+ 3 Ine ndapereka lamulo kwa opatulika anga.+ Ndaitananso anthu anga amphamvu oti asonyeze mkwiyo wanga.+ Amenewa ndi anthu anga okondwa kwambiri. 4 Tamverani! M’mapiri mukumveka phokoso la khamu la anthu, phokoso ngati la anthu ambiri.+ Tamverani! Kukumveka chisokonezo cha maufumu, cha mitundu imene yasonkhanitsidwa pamodzi.+ Yehova wa makamu akusonkhanitsira asilikali ku nkhondo.+ 5 Iwo akuchokera kudziko lakutali.+ Akuchokera kumalekezero a kumwamba. Yehova akubwera ndi zida za mkwiyo wake, kuti asakaze dziko lonse lapansi.+
6 “Fuulani, anthu inu,+ chifukwa tsiku la Yehova lili pafupi.+ Lidzabwera ngati kuti Wamphamvuyonse akulanda zinthu.+ 7 N’chifukwa chake anthu onse adzataya mtima, ndipo mitima ya anthu onse idzasungunuka.+ 8 Anthu asokonezeka.+ Nsautso ndi zowawa za pobereka zawagwera. Iwo akumva zowawa ngati mkazi amene akubereka.+ Akuyang’anana modabwa. Nkhope zawo zafiira ndi mantha.+
9 “Taonani! Tsiku la Yehova likubwera. Tsikulo n’lankhanza, laukali ndiponso lamkwiyo woyaka moto. Likubwera kuti lidzachititse dziko kukhala chinthu chodabwitsa,+ ndiponso kuti lidzawononge anthu ochimwa a m’dzikolo.+ 10 Pakuti nyenyezi zakumwamba ndi magulu a nyenyezi a Kesili+ sizidzawala. Dzuwa lidzachita mdima potuluka, ndipo mwezi sudzaonetsa kuwala kwake. 11 Nthaka ndidzaibwezera zoipa zake,+ ndipo anthu oipa ndidzawabwezera zolakwa zawo. Kunyada kwa anthu odzikuza ndidzakuthetsa, ndipo ndidzatsitsa olamulira ankhanza ndi odzikweza.+ 12 Ndidzachititsa kuti anthu azisowa kwambiri kuposa golide woyengedwa bwino,+ ndiponso ndidzachititsa kuti anthu ochokera kufumbi azisowa kwambiri kuposa golide wa ku Ofiri.+ 13 Chifukwa cha zimenezi, ndidzachititsa kuti kumwamba kugwedezeke+ ndipo dziko lapansi lidzanjenjemera n’kuchoka m’malo mwake, chifukwa cha ukali wa Yehova wa makamu,+ pa tsiku limene mkwiyo wake udzayake.+ 14 Monga insa imene ikuthamangitsidwa ndiponso monga ziweto zopanda wozikusa,+ aliyense wa iwo adzatembenukira kwa anthu ake, ndipo aliyense wa iwo adzathawira kudziko lake.+ 15 Aliyense amene adzapezedwe adzabooledwa ndipo aliyense amene adzagwidwe limodzi ndi anthu ena onse pa nthawiyo, adzaphedwa ndi lupanga.+ 16 Ana awo adzaphwanyidwaphwanyidwa, iwo akuona.+ Katundu wa m’nyumba zawo adzalandidwa, ndipo akazi awo adzagwiriridwa.+
17 “Ndidzachititsa Amedi kuti awaukire.+ Iwowa amaona kuti siliva si kanthu, ndipo sasangalala ndi golide. 18 Ndi mauta awo, adzaphwanyaphwanya ngakhale anyamata awo.+ Iwo sadzamvera chisoni zipatso za m’mimba.+ Diso lawo silidzamvera chisoni ana aamuna. 19 Babulo, amene ndi chokongoletsera maufumu,+ chinthu chokongola ndi chonyadira cha Akasidi,+ adzakhala ngati pamene Mulungu anagonjetsa Sodomu ndi Gomora.+ 20 M’Babulo simudzakhalanso anthu,+ ndipo iye sadzakhalaponso ku mibadwomibadwo.+ Kumeneko Mluya sadzakhomako hema wake, ndipo abusa sadzagonekako ziweto zawo. 21 Nyama zam’tchire zokhala kumadera opanda madzi zidzagona kumeneko, ndipo nyumba za anthu amene anali kukhala kumeneko zidzadzaza ndi akadzidzi.+ Nthiwatiwa zizidzakhala kumeneko, ndipo ziwanda zooneka ngati mbuzi* zizidzadumphadumpha kumeneko.+ 22 Mimbulu izidzalira munsanja zake zokhalamo,+ ndipo njoka zikuluzikulu zizidzakhala m’nyumba zachifumu zokongola. Nyengo yake yatsala pang’ono kufika, ndipo masiku ake sadzatalikitsidwa.”+