16 Koma ine ndinawayankha kuti, Aroma sachita zinthu mwa njira imeneyo. Iwo sapereka munthu m’manja mwa omuneneza pongofuna kuwakondweretsa, munthu wonenezedwayo+ asanapatsidwe mwayi woonana pamasom’pamaso ndi omunenezawo kuti alankhule mawu odziteteza pa mlanduwo.