Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Chivumbulutso 8:7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 7 Mngelo woyamba analiza lipenga lake. Atatero, panaoneka matalala ndi moto,+ zosakanikirana ndi magazi. Zimenezi zinaponyedwa kudziko lapansi. Ndipo gawo limodzi mwa magawo atatu a dziko lapansi linapsa.+ Kuwonjezera pamenepo, gawo limodzi mwa magawo atatu a mitengo linapsa, komanso zomera zonse zobiriwira+ zinapsa.

  • Chivumbulutso 8:8
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 8 Kenako mngelo wachiwiri analiza lipenga lake. Ndipo chinachake chokhala ngati phiri lalikulu+ limene likuyaka moto chinaponyedwa m’nyanja.+ Moti gawo limodzi mwa magawo atatu a nyanja, linasanduka magazi.+

  • Chivumbulutso 8:10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Tsopano mngelo wachitatu analiza lipenga lake. Ndipo nyenyezi yaikulu yoyaka ngati nyale inagwa kuchokera kumwamba.+ Inagwera pa gawo limodzi mwa magawo atatu a mitsinje, ndi pa akasupe a madzi.+

  • Chivumbulutso 8:12
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 Ndiyeno mngelo wachinayi analiza lipenga lake. Atatero, gawo limodzi mwa magawo atatu a dzuwa linakanthidwa. Chimodzimodzinso gawo limodzi mwa magawo atatu a mwezi, ndi a nyenyezi. Zinatero kuti gawo limodzi mwa magawo atatu a zimenezi lichite mdima, ndi kuti gawo limodzi mwa magawo atatu a usana+ lisalandire kuunika,+ chimodzimodzinso usiku.

  • Chivumbulutso 9:1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 Kenako mngelo wachisanu analiza lipenga+ lake. Ndipo ndinaona nyenyezi+ imene inagwera kudziko lapansi kuchokera kumwamba. Nyenyeziyo inapatsidwa kiyi+ wa dzenje+ lolowera kuphompho.

  • Chivumbulutso 9:13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 13 Kenako mngelo wa 6+ analiza lipenga+ lake. Ndipo ndinamva mawu amodzi+ kuchokera panyanga za paguwa lansembe lagolide+ lokhala pamaso pa Mulungu.

  • Chivumbulutso 11:15
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 15 Mngelo wa 7 analiza lipenga+ lake. Ndipo kumwamba kunamveka mawu osiyanasiyana, akunena mokweza kuti: “Ufumu wa dziko wakhala ufumu wa Ambuye wathu+ ndi wa Khristu wake.+ Iye adzalamulira monga mfumu kwamuyaya.”+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena