Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 2 Mafumu 22:18, 19
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 18 Mfumu ya Yuda imene yakutumani kuti mudzafunse kwa Yehova, mukaiuze kuti, “Yehova Mulungu wa Isiraeli wanena kuti: ‘Ponena za mawu amene wamvawo, 19 chifukwa chakuti mtima wako unali womvera* ndipo unadzichepetsa+ pamaso pa Yehova utamva zimene ndanena zokhudza malo ano ndi anthu ake, kuti malowa adzakhala chinthu chodabwitsa ndi temberero ndipo unangʼamba zovala zako+ nʼkuyamba kulira pamaso panga, ineyo ndamva, watero Yehova.

  • 2 Mbiri 33:13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 13 Manase anayamba kupemphera kwa Mulungu ndipo iye anamva pemphero lake lochonderera ndiponso lopempha chifundo. Kenako anamʼbwezera ku Yerusalemu ndipo anakhalanso mfumu.+ Zitatero, Manase anadziwa kuti Yehova ndi Mulungu woona.+

  • Salimo 22:24
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 24 Chifukwa iye sananyoze kapena kunyansidwa ndi kuvutika kwa munthu woponderezedwa.+

      Sanabise nkhope yake kwa iye.+

      Pamene anamulirira kuti amuthandize, iye anamva.+

  • Salimo 34:18
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 18 Yehova ali pafupi ndi anthu a mtima wosweka.+

      Iye amapulumutsa anthu amene akudzimvera chisoni mumtima mwawo.*+

  • Miyambo 28:13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 13 Wobisa machimo ake zinthu sizidzamuyendera bwino,+

      Koma amene amawaulula nʼkuwasiya adzachitiridwa chifundo.+

  • Yesaya 57:15
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 15 Chifukwa Wapamwamba ndi Wokwezeka,

      Amene adzakhalepo mpaka kalekale+ ndiponso dzina lake ndi loyera,+ wanena kuti:

      “Ine ndimakhala pamalo apamwamba komanso oyera,+

      Koma ndimakhalanso ndi anthu opsinjika ndiponso amene ali ndi mtima wodzichepetsa,

      Kuti nditsitsimutse mtima wa anthu onyozeka

      Ndiponso kuti nditsitsimutse mtima wa anthu opsinjika.+

  • Luka 15:22-24
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 22 Koma bambowo anauza akapolo ake kuti, ‘Fulumirani, tengani mkanjo wabwino kwambiri uja mumuveke. Mumuvekenso mphete kudzanja lake ndi nsapato kumapazi kwake. 23 Komanso mubweretse mwana wa ngʼombe wamphongo wonenepa, mumuphe ndipo tidye ndi kusangalala. 24 Chifukwa mwana wangayu anali wakufa koma tsopano wakhalanso ndi moyo,+ anatayika koma wapezeka.’ Choncho onse anayamba kusangalala.

  • Luka 18:13, 14
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 13 Koma wokhometsa msonkho uja, ataima chapatali ndithu, sanafune ngakhale kukweza maso ake kumwamba. Iye ankangodziguguda pachifuwa nʼkumanena kuti, ‘Mulungu wanga, ndikomereni mtima* munthu wochimwa ine.’+ 14 Ndithu ndikukuuzani, munthu ameneyu anapita kwawo ataonedwa kuti ndi wolungama kwambiri kuposa Mfarisi uja.+ Chifukwa aliyense wodzikweza adzachititsidwa manyazi, koma aliyense amene amadzichepetsa adzakwezedwa.”+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena