Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Salimo 45:6
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  6 Mulungu ndi mpando wako wachifumu mpaka kalekale.+

      Ndodo ya ufumu wako ndi ndodo yachilungamo.+

  • Salimo 72:1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 72 Inu Mulungu, thandizani mfumu kuti iziweruza mogwirizana ndi zigamulo zanu,

      Ndipo dziwitsani mwana wa mfumu za chilungamo chanu.+

  • Yesaya 9:7
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  7 Ulamuliro* wake udzafika kutali

      Ndipo mtendere sudzatha,+

      Pampando wachifumu wa Davide+ ndiponso mu ufumu wake

      Kuti iye achititse ufumuwo kukhazikika+ ndiponso kukhala wolimba

      Pogwiritsa ntchito chilungamo+ ndiponso mtima wowongoka,+

      Kuyambira panopa mpaka kalekale.

      Yehova wa magulu ankhondo akumwamba adzachita zimenezi modzipereka kwambiri.

  • Yesaya 11:4, 5
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  4 Adzaweruza mwachilungamo anthu onyozeka,

      Ndipo adzadzudzula anthu mowongoka mtima, pothandiza ofatsa apadziko lapansi.

      Adzakwapula dziko lapansi ndi ndodo ya pakamwa pake+

      Ndipo adzapha anthu oipa pogwiritsa ntchito mpweya* wamʼkamwa mwake.+

       5 Chilungamo ndi kukhulupirika

      Zidzakhala lamba wamʼchiuno mwake.+

  • Yeremiya 23:5
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 5 “Taonani! Masiku adzafika,” watero Yehova, “pamene ndidzaike mfumu yolungama pampando wachifumu yochokera mʼbanja lachifumu la Davide.*+ Mfumuyo idzalamulira mʼdzikoli+ ndipo idzachita zinthu mwanzeru, motsatira malamulo komanso mwachilungamo.+

  • Zekariya 9:9
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    •  9 Iwe mwana wamkazi wa Ziyoni* sangalala kwambiri.

      Fuula mokondwera iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu.*

      Taona, mfumu yako ikubwera kwa iwe.+

      Mfumuyo ndi yolungama ndipo ikubweretsa chipulumutso.*

      Ndi yodzichepetsa+ ndipo ikubwera itakwera bulu.

      Ikubwera itakwera mwana wamphongo wa bulu.+

  • Aheberi 1:9
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 9 Unkakonda chilungamo ndipo unkadana ndi kusamvera malamulo. Nʼchifukwa chake Mulungu, Mulungu wako, anakudzoza+ ndi mafuta achisangalalo chachikulu kuposa mafumu anzako.”+

  • Chivumbulutso 19:11
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 11 Ndinaona kumwamba kutatseguka, kenako ndinaona hatchi yoyera.+ Amene anakwera pahatchiyo dzina lake linali lakuti Wokhulupirika+ ndi Woona.+ Iye amaweruza molungama ndipo akumenya nkhondo mwachilungamo.+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena