-
Maliko 6:1-6Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
6 Kenako anachoka kumeneko nʼkufika mʼdera lakwawo+ ndipo ophunzira ake anamʼtsatira. 2 Sabata litakwana, iye anayamba kuphunzitsa musunagoge. Anthu ambiri amene anamumvetsera anadabwa ndipo ananena kuti: “Kodi munthu ameneyu anazitenga kuti zinthu zimenezi?+ Ndipo nʼchifukwa chiyani nzeru zimenezi zinaperekedwa kwa iyeyu, komanso kuti azitha kuchita ntchito zamphamvu zoterezi?+ 3 Kodi iyeyu si kalipentala,+ mwana wa Mariya,+ komanso mchimwene wake wa Yakobo,+ Yosefe, Yudasi ndi Simoni?+ Ndipo azichemwali ake si awa tili nawo pompano?” Choncho anayamba kukhumudwa naye. 4 Koma Yesu anawauza kuti: “Mneneri salemekezedwa kwawo, ngakhale ndi achibale ake, ngakhale mʼnyumba mwake momwe, koma kwina.”+ 5 Choncho sanathe kuchita ntchito zamphamvu zilizonse kumeneko, koma anangoika manja pa odwala owerengeka nʼkuwachiritsa. 6 Ndithudi, iye anadabwa kuona kuti anthuwo analibe chikhulupiriro. Choncho anazungulira mʼmidzi yapafupi nʼkumaphunzitsa anthu.+
-