3 Winawake akufuula mʼchipululu kuti:
“Konzani njira ya Yehova!+
Mulungu wathu mukonzereni msewu wowongoka+ wodutsa mʼchipululu.+
4 Chigwa chilichonse chikwezedwe mʼmwamba,
Ndipo phiri lililonse ndi chitunda chilichonse zitsitsidwe.
Malo okumbikakumbika asalazidwe,
Ndipo malo azitunda akhale chigwa.+
5 Ulemerero wa Yehova udzaonekera,+
Ndipo anthu onse adzauonera limodzi,+
Chifukwa pakamwa pa Yehova panena.”