Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Mateyu 3:1
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 Mʼmasiku amenewo, Yohane+ Mʼbatizi anapita mʼchipululu cha Yudeya nʼkuyamba kulalikira.+

  • Mateyu 3:3
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 Mneneri Yesaya ananeneratu za iyeyu+ mʼmawu awa: “Winawake akufuula mʼchipululu kuti: ‘Konzani njira ya Yehova!* Muwongole misewu yake.’”+

  • Maliko 1:2-4
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 2 Mogwirizana ndi zimene zinalembedwa mʼbuku la mneneri Yesaya kuti: “(Taona! Ine ndikutumiza mthenga wanga kuti atsogole* kukakukonzera njira.)*+ 3 Winawake akufuula mʼchipululu kuti: ‘Konzani njira ya Yehova!* Muwongole misewu yake.’”+ 4 Yohane Mʼbatizi anali mʼchipululu ndipo ankalalikira za ubatizo monga chizindikiro cha kulapa kuti machimo akhululukidwe.+

  • Luka 3:3-6
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 3 Choncho iye anapita mʼmidzi yonse yapafupi ndi Yorodano ndipo ankalalikira za ubatizo monga chizindikiro cha kulapa kuti machimo akhululukidwe.+ 4 Ankachita zimenezi mogwirizana ndi zimene zinalembedwa mʼbuku la mawu a Mneneri Yesaya kuti: “Winawake akufuula mʼchipululu kuti: ‘Konzani njira ya Yehova!* Muwongole misewu yake.+ 5 Chigwa chilichonse chikwiriridwe, ndipo phiri lililonse ndi chitunda chilichonse zisalazidwe. Njira zokhotakhota zikhale zowongoka ndipo malo okumbikakumbika akhale osalaza bwino. 6 Anthu onse adzaona njira ya Mulungu yopulumutsira anthu.’”+

  • Yohane 1:23
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 23 Iye anati: “Ndine mawu a winawake amene akufuula mʼchipululu kuti, ‘Wongolani njira ya Yehova,’*+ monga mmene mneneri Yesaya ananenera.”+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena