Mateyu
4 Kenako mzimu unatsogolera Yesu kuchipululu+ kuti akayesedwe+ ndi Mdyerekezi. 2 Atasala kudya masiku 40 usana ndi usiku,+ anamva njala. 3 Ndiyeno Woyesayo+ anabwera n’kumuuza kuti: “Ngati ndinudi mwana wa Mulungu,+ uzani miyala iyi kuti isanduke mitanda ya mkate.” 4 Koma poyankha iye anati: “Malemba amati, ‘Munthu sangakhale ndi moyo ndi chakudya chokha, koma ndi mawu onse otuluka pakamwa pa Yehova.’”*+
5 Kenako Mdyerekezi anamutenga ndi kupita naye mumzinda woyera,+ ndipo anamukweza pamwamba pa khoma la mpanda wa kachisi 6 n’kumuuza kuti: “Ngati ndinu mwana wa Mulungu, mudziponye pansi,+ pajatu Malemba amati, ‘Iye adzalamula angelo ake za inu, ndipo adzakunyamulani m’manja mwawo, kuti phazi lanu lisawombe mwala uliwonse.’”+ 7 Koma Yesu anamuyankha kuti: “Malemba amatinso, ‘Usamuyese Yehova Mulungu wako.’”+
8 Ndiyeno Mdyerekezi anamutenganso ndi kupita naye paphiri lalitali kwambiri, ndipo anamuonetsa maufumu onse a padziko+ ndi ulemerero wawo. 9 Kenako anamuuza kuti: “Ndikupatsani zinthu zonsezi+ ngati mutangogwada pansi n’kundiweramira kamodzi kokha.”+ 10 Koma Yesu anamuyankha kuti: “Choka Satana! Pakuti Malemba amati, ‘Yehova Mulungu wako ndi amene uyenera kumulambira,+ ndipo uyenera kutumikira+ iye yekha basi.’”+ 11 Pamenepo Mdyerekezi uja anamusiya,+ ndipo kunabwera angelo ndi kuyamba kum’tumikira.+
12 Tsopano Yesu atamva kuti Yohane amugwira,+ anachoka kumeneko ndipo anapita ku Galileya.+ 13 Komanso atachoka ku Nazareti, anafika ku Kaperenao+ n’kupeza malo okhala m’mphepete mwa nyanja m’zigawo za Zebuloni ndi Nafitali,+ 14 kuti mawu amene ananenedwa kudzera mwa Yesaya mneneri akwaniritsidwe. Iye ananena kuti: 15 “Anthu okhala m’dziko la Zebuloni ndi dziko la Nafitali, m’mbali mwa msewu wa kunyanja kutsidya lina la Yorodano, ku Galileya+ kumene kunali kukhala anthu a mitundu ina, 16 anthu okhala mu mdima+ anaona kuwala kwakukulu,+ ndipo anthu okhala m’dera la mthunzi wa imfa, kuwala+ kunawatulukira.”+ 17 Kuyambira nthawi imeneyo, Yesu anayamba kulalikira ndi kunena kuti: “Lapani+ anthu inu, pakuti ufumu+ wakumwamba wayandikira.”
18 Pamene anali kuyenda m’mbali mwa nyanja ya Galileya,* Yesu anaona amuna awiri apachibale akuponya ukonde wophera nsomba m’nyanja, pakuti anali asodzi. Mayina awo anali Simoni+ wotchedwa Petulo+ ndi Andireya. 19 Iye anawauza kuti: “Nditsatireni, ndipo ndikusandutsani asodzi a anthu.”+ 20 Nthawi yomweyo iwo anasiya maukonde awo+ n’kumutsatira. 21 Atapitirira pamenepo, anaona amuna enanso awiri+ apachibale, Yakobo mwana wa Zebedayo, ndi m’bale wake Yohane. Iwo anali m’ngalawa limodzi ndi bambo awo, a Zebedayo,+ akusoka maukonde awo, ndipo anawaitana. 22 Nthawi yomweyo anasiya ngalawa ija ndi bambo awo n’kumutsatira.
23 Atatero, anayendayenda+ m’Galileya+ yense kuphunzitsa m’masunagoge+ mwawo, kulalikira uthenga wabwino wa ufumu ndi kuchiritsa anthu matenda amtundu uliwonse+ ndi zofooka zilizonse. 24 Choncho mbiri yake inafalikira mu Siriya+ monse. Anthu anamubweretsera onse amene sanali kumva bwino m’thupi,+ amene anali kuvutika ndi matenda komanso zowawa zamitundumitundu, ogwidwa ndi ziwanda, akhunyu,+ ndi anthu akufa ziwalo, ndipo iye anawachiritsa. 25 Chotero makamu a anthu ambiri ochokera ku Galileya,+ ku Dekapole, ku Yerusalemu,+ ku Yudeya komanso ochokera kutsidya lina la Yorodano, anam’tsatira.