1 Akorinto
2 Chotero abale, pamene ndinafika kwa inu kudzalengeza za chinsinsi chopatulika+ cha Mulungu, sindinafike ndi malankhulidwe+ adzaoneni kapena ndi nzeru zodabwitsa. 2 Pakuti ndinasankha kuti pamene ndili pakati panu ndisadziwe china chilichonse kupatulapo Yesu Khristu,+ amene anapachikidwa. 3 Choncho ndinafika kwa inu ndili wofooka, ndipo ndinali kunjenjemera+ ndi mantha. 4 Polankhula ndi polalikira, mawu anga sanali okopa, oonetsa nzeru, koma oonetsa mzimu ndi mphamvu,+ 5 kuti chikhulupiriro chanu chisazikike pa nzeru za anthu,+ koma pa mphamvu ya Mulungu.+
6 Tsopano tikulankhula za nzeru kwa anthu okhwima mwauzimu,+ koma osati nzeru+ ya nthawi ino kapena ya olamulira a nthawi* ino+ amene adzawonongedwa.+ 7 Koma tikulankhula za nzeru ya Mulungu imene inaonekera m’chinsinsi chopatulika,+ nzeru yobisika. Mulungu anakonzeratu zochita zimenezi kusanakhale nthawi* zosiyanasiyana,+ kuti tikhale ndi ulemerero. 8 Palibe wolamulira+ ndi mmodzi yemwe wa nthawi* ino amene anadziwa+ nzeru imeneyi, chifukwa ngati anali kuidziwa sakanapachika+ Ambuye waulemereroyo. 9 Koma monga mmene Malemba amanenera: “Palibe munthu amene anaonapo kapena kumvapo kapenanso kuganizapo zimene Mulungu wakonzera omukonda.”+ 10 Pakuti mwa mzimu+ wake, Mulungu anaululira+ ifeyo zinthu zimenezi, chifukwa mzimu+ umafufuza zinthu zonse, ngakhale zinthu zozama+ za Mulungu.
11 Kodi ndi munthu uti amene angadziwe za munthu kupatulapo mzimu+ umene uli mwa munthuyo? Momwemonso, palibe amene akudziwa zinthu za Mulungu, kupatulapo mzimu+ wa Mulungu. 12 Tsopano sitinalandire mzimu+ wa dziko, koma mzimu+ wochokera kwa Mulungu, kuti tidziwe zinthu zimene Mulungu watipatsa mokoma mtima.+ 13 Timalankhulanso zinthu zimenezi, osati ndi mawu ophunzitsidwa ndi nzeru za anthu,+ koma ndi mawu amene mzimu+ watiphunzitsa, pamene tikuphatikiza zochitika zauzimu ndi mawu auzimu.+
14 Koma munthu wokonda zinthu za m’dziko* salandira zinthu za mzimu wa Mulungu, chifukwa amaziona ngati zopusa ndipo sangathe kuzidziwa,+ chifukwa zimafuna kuzifufuza mwauzimu. 15 Komano munthu wauzimu+ amafufuza zinthu zonse, koma iye safufuzidwa+ ndi munthu aliyense. 16 Pakuti “ndani akudziwa maganizo a Yehova+ kuti amulangize?”+ Koma ifeyo tili ndi maganizo+ a Khristu.