-
Yeremiya 49:19Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
19 “Taona! Wina adzabwera ngati mkango+ kuchokera m’nkhalango zowirira za m’mphepete mwa Yorodano. Iye adzafika pamalo otetezeka+ odyetsera nkhosa koma m’kanthawi kochepa ndidzamuthamangitsa pamalowo.+ Ndidzasankha ndi kuika woyang’anira malowo, pakuti ndani angafanane ndi ine,+ ndipo ndani angalimbane ndi ine,+ komanso ndi m’busa uti tsopano amene angatsutsane nane?+
-
-
Yeremiya 50:44Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
44 “Taona! Wina adzabwera ngati mkango kuchokera m’nkhalango zowirira za m’mphepete mwa Yorodano.+ Iye adzafika pamalo otetezeka odyetsera nkhosa koma m’kanthawi kochepa ndidzathamangitsa eni malowo.+ Ndidzasankha ndi kuika woyang’anira malowo,+ pakuti ndani angafanane ndi ine,+ ndipo ndani angalimbane ndi ine,+ komanso ndi m’busa uti tsopano amene angatsutsane nane?+
-