28 Komanso, Mulungu anawadalitsa+ n’kuwauza kuti: “Muberekane,+ muchuluke, mudzaze dziko lapansi, ndipo muliyang’anire.+ Muyang’anirenso+ nsomba zam’nyanja ndi zolengedwa zouluka m’mlengalenga, komanso cholengedwa chilichonse chokwawa padziko lapansi.”