-
Esitere 3:12Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
12 Kenako anaitana alembi a mfumu+ m’mwezi woyamba, pa tsiku la 13 la mweziwo. Ndipo alembiwo analemba+ zonse zimene Hamani analamula masatarapi* a mfumu, abwanamkubwa a m’zigawo zosiyanasiyana+ za ufumuwo ndi akalonga a anthu osiyanasiyana m’chigawo chilichonse. Makalata amenewa anawalemba malinga ndi mmene anthu a m’chigawo chilichonse anali kulembera+ ndiponso m’chinenero chawo. Makalatawa anawalemba m’dzina+ la Mfumu Ahasiwero ndipo anawadinda ndi mphete yake yodindira.+
-
-
Esitere 8:5Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
-
-
5 Tsopano Esitere anati: “Ngati zingakukomereni mfumu, ndipo ngati mungandikomere mtima,+ komanso ngati n’zoyenera kwa inu mfumu ndiponso ngati ndine munthu wabwino kwa inu, palembedwe makalata ofafaniza makalata+ achiwembu amene Hamani, mwana wa Hamedata Mwagagi,+ analemba pofuna kuwononga Ayuda+ amene ali m’zigawo zanu zonse mfumu.+
-