1 Mbiri
24 Tsopano anagawa ana a Aroni m’magulu awo. Ana a Aroni anali Nadabu,+ Abihu,+ Eleazara,+ ndi Itamara.+ 2 Nadabu ndi Abihu+ anamwalira opanda ana aamuna bambo awo akali ndi moyo,+ koma Eleazara+ ndi Itamara anapitiriza kukhala ansembe. 3 Davide ndi Zadoki,+ yemwe anali wochokera mwa ana a Eleazara, ndiponso Ahimeleki,+ wochokera mwa ana a Itamara, anagawa ana a Aroniwo m’magulu a udindo pa utumiki wawo.+ 4 Koma ana a Eleazara anapezeka kuti anali ndi atsogoleri ambiri kuposa ana a Itamara. Choncho ana a Eleazara, omwe anali atsogoleri a nyumba za makolo awo, anawagawa m’magulu 16. Ndiponso ana a Itamara, omwe anali atsogoleri a nyumba za makolo awo, anawagawa m’magulu 8.
5 Pogawapo, anachita maere+ panyumba ya Eleazara pamodzi ndi panyumba ya Itamara. Anachita zimenezi chifukwa chakuti panafunika atsogoleri a pamalo oyera,+ ndi atsogoleri otumikira Mulungu woona, ochokera mwa ana a Eleazara ndiponso ochokera mwa ana a Itamara. 6 Kenako Semaya mwana wa Netaneli mlembi+ wa Alevi, anawalemba mayina pamaso pa mfumu, akalonga, wansembe Zadoki,+ Ahimeleki+ mwana wa Abiyatara,+ ndiponso pamaso pa atsogoleri a nyumba za makolo za ansembe ndi za Alevi.+ Anali kutenga nyumba imodzi ya makolo ya Eleazara+ ndi nyumba imodzi ya makolo ya Itamara.+
7 Atachita maere, zotsatira zake zinali motere: Woyamba anali Yehoyaribu,+ wachiwiri Yedaya, 8 wachitatu Harimu, wachinayi Seorimu, 9 wachisanu Malikiya, wa 6 Miyamini, 10 wa 7 Hakozi, wa 8 Abiya,+ 11 wa 9 Yesuwa, wa 10 Sekaniya, 12 wa 11 Eliyasibu, wa 12 Yakimu, 13 wa 13 Hupa, wa 14 Yesebeabu, 14 wa 15 Biliga, wa 16 Imeri, 15 wa 17 Heziri, wa 18 Hapizezi, 16 wa 19 Petahiya, wa 20 Yehezikeli, 17 wa 21 Yakini, wa 22 Gamuli, 18 wa 23 Delaya, ndipo wa 24 anali Maaziya.
19 Limeneli ndilo linali dongosolo+ la utumiki wawo,+ kuti azilowa m’nyumba ya Yehova malinga ndi mphamvu imene anapatsidwa+ kudzera m’dzanja la Aroni kholo lawo, monga mmene Yehova Mulungu wa Isiraeli anamulamulira.
20 Ana a Levi amene anatsala anali motere: Pa ana a Amuramu+ panali Subaeli.+ Pa ana a Subaeli panali Yedeya. 21 Panalinso Rehabiya:+ Pa ana a Rehabiya panali Isiya mtsogoleri wawo. 22 Mwa mbadwa za Izara,+ panali Selomoti.+ Pa ana a Selomoti panali Yahati. 23 Ana a Heburoni+ anali Yeriya+ mtsogoleri wawo, Amariya wachiwiri, Yahazieli wachitatu, ndi Yekameamu wachinayi. 24 Pa ana a Uziyeli panali Mika. Pa ana a Mika+ panali Samiri. 25 M’bale wake wa Mika anali Isiya, ndipo pa ana a Isiya panali Zekariya.
26 Ana a Merari+ anali Mali+ ndi Musi.+ Pa ana a Yaaziya panali Beno. 27 Pa ana a Merari panali Yaaziya. Ana a Yaaziya anali Beno, Sohamu, Zakuri, ndi Ibiri. 28 Pa ana a Mali panali Eleazara amene analibe mwana.+ 29 Panalinso Kisi: Pa ana a Kisi panali Yerameeli. 30 Ana a Musi anali Mali,+ Ederi, ndi Yerimoti.+
Amenewa anali ana a Alevi potsata nyumba za makolo awo.+ 31 Iwonso anachita maere+ mofanana ndi mmene abale awo, ana a Aroni, anachitira pamaso pa Davide mfumu, Zadoki, Ahimeleki, ndiponso pamaso pa atsogoleri a nyumba za makolo za ansembe ndi za Alevi. Nyumba ya makolo+ ya wamkulu inali chimodzimodzi ndi nyumba ya makolo ya wamng’ono.