Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • 1 Mafumu 19:10
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 10 Iye anayankha kuti: “Ine ndakutumikirani modzipereka kwambiri inu Yehova Mulungu wa magulu ankhondo akumwamba,+ koma Aisiraeli asiya pangano lanu.+ Agwetsa maguwa anu ansembe ndipo apha aneneri anu ndi lupanga,+ moti ine ndatsala ndekhandekha. Tsopano ayambanso kundifunafuna kuti andiphe.”+

  • Salimo 119:139
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 139 Kudzipereka kwanga kwa inu kuli ngati moto umene ukuyaka mumtima mwanga,+

      Chifukwa adani anga aiwala mawu anu.

  • Mateyu 21:12, 13
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 12 Kenako Yesu analowa mʼkachisi nʼkuthamangitsa anthu onse amene ankagulitsa ndi kugula zinthu mʼkachisimo, ndipo anagubuduza matebulo a anthu amene ankasintha ndalama komanso mabenchi a anthu amene ankagulitsa nkhunda.+ 13 Iye anawauza kuti: “Malemba amati, ‘Nyumba yanga idzatchedwa nyumba yopemphereramo,’+ koma inu mukuisandutsa phanga la achifwamba.”+

  • Maliko 11:15-17
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 15 Tsopano iwo anafika ku Yerusalemu. Kumeneko analowa mʼkachisi nʼkuyamba kuthamangitsa anthu amene ankagulitsa ndi kugula zinthu mʼkachisimo, ndipo anagubuduza matebulo a anthu amene ankasintha ndalama komanso mabenchi a anthu amene ankagulitsa nkhunda.+ 16 Iye sanalole aliyense kuti adutse mʼkachisimo atanyamula katundu. 17 Iye ankaphunzitsa ndipo ankauza anthuwo kuti: “Kodi Malemba sanena kuti, ‘Nyumba yanga idzatchedwa nyumba yopemphereramo anthu a mitundu yonseʼ?+ Koma inu mwaisandutsa phanga la achifwamba.”+

  • Yohane 2:13-17
    Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
    • 13 Tsopano Pasika+ wa Ayuda anali atayandikira, choncho Yesu ananyamuka nʼkupita ku Yerusalemu. 14 Kumeneko anapeza ogulitsa ngʼombe, nkhosa ndi nkhunda+ komanso osintha ndalama ali mʼkachisi atakhala mʼmipando yawo. 15 Choncho anapanga chikwapu chazingwe nʼkuthamangitsa onse amene anali ndi nkhosa komanso ngʼombe mʼkachisimo. Anakhuthula makobidi a anthu osintha ndalama nʼkugubuduza matebulo awo.+ 16 Ndiyeno anauza ogulitsa nkhundawo kuti: “Chotsani izi muno! Musiyiretu kusandutsa nyumba ya Atate wanga kukhala nyumba ya malonda!”*+ 17 Ophunzira ake anakumbukira zimene Malemba amanena kuti: “Kudzipereka kwanga panyumba yanu kudzakhala ngati moto umene ukuyaka mumtima mwanga.”+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena