Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Machitidwe 26
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

Zimene Zili Mʼbuku la Machitidwe

      • Paulo anadziteteza pamaso pa Agiripa (1-11)

      • Paulo anafotokoza mmene anakhalira Mkhristu (12-23)

      • Zimene Fesito ndi Agiripa anachita (24-32)

Machitidwe 26:1

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 25:13

Machitidwe 26:2

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 24:5, 9

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    11/15/2003, ptsa. 15-16

Machitidwe 26:3

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    11/15/2003, ptsa. 15-16

Machitidwe 26:4

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Aga 1:13, 14

Machitidwe 26:5

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 23:6; Afi 3:4, 5
  • +Mac 22:3

Machitidwe 26:6

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 24:15

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Kuchitira Umboni Mokwanira, ptsa. 198-199

Machitidwe 26:7

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 24:20, 21

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Kuchitira Umboni Mokwanira, tsa. 199

Machitidwe 26:9

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    6/15/1999, ptsa. 29-31

Machitidwe 26:10

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Yoh 16:2; Mac 8:3; 1Ak 15:9; Aga 1:13; 1Ti 1:13
  • +Mac 9:1, 2, 14

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    6/15/1999, tsa. 30

Machitidwe 26:11

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    6/15/1999, ptsa. 30-31

Machitidwe 26:13

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 9:3-5; 22:6-8

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Kuchitira Umboni Mokwanira, tsa. 200

Machitidwe 26:14

Mawu a M'munsi

  • *

    Zimenezi zinali ndodo zosongola zimene ankatosera nyama zapagoli kuti ziziyenda mofulumira.

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Kuchitira Umboni Mokwanira, ptsa. 199-200

    Baibulo la Dziko Latsopano (nwt), tsa. 2145

    Nsanja ya Olonda,

    8/1/2011, tsa. 23

    10/1/2003, tsa. 32

    9/1/1998, tsa. 30

    6/15/1990, tsa. 24

Machitidwe 26:16

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 22:14, 15; Aga 1:11, 12; 1Ti 1:12

Machitidwe 26:17

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 22:21; Aro 11:13

Machitidwe 26:18

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Yes 61:1
  • +Akl 1:13
  • +Yoh 8:12; 2Ak 4:6
  • +Aef 2:1, 2
  • +1Yo 3:5

Machitidwe 26:20

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 9:22
  • +Mac 9:28
  • +Mt 3:8

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Kuchitira Umboni Mokwanira, ptsa. 200-201

Machitidwe 26:21

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 21:30, 31

Machitidwe 26:22

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Lu 24:27, 44; Aro 3:21

Machitidwe 26:23

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Sl 22:7; 35:19; Yes 50:6; 53:5
  • +Sl 16:10
  • +Sl 18:49; Yes 11:10; Lu 2:30-32

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Kukhala ndi Moyo Kosatha, tsa. 172

Machitidwe 26:24

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Kuchitira Umboni Mokwanira, tsa. 202

    Nsanja ya Olonda,

    12/15/2001, tsa. 24

Machitidwe 26:26

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Yoh 18:20

Machitidwe 26:27

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Nsanja ya Olonda,

    11/15/2003, ptsa. 16-17

Machitidwe 26:28

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Kuchitira Umboni Mokwanira, tsa. 202

    Nsanja ya Olonda,

    11/15/2003, ptsa. 16-17

Machitidwe 26:30

Kalozera

  • Buku Lofufuzira Nkhani

    Kuchitira Umboni Mokwanira, tsa. 202

Machitidwe 26:31

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 23:26, 29; 25:24, 25

Machitidwe 26:32

Malifalensi Opezeka Pakati pa Tsamba

  • +Mac 25:11, 12

Mabaibulo Ena

Dinani pa nambala ya vesi kuti muone mavesi a m'Baibulo lina ofanana ndi vesilo.

Malemba Ena

Mac. 26:1Mac 25:13
Mac. 26:2Mac 24:5, 9
Mac. 26:4Aga 1:13, 14
Mac. 26:5Mac 23:6; Afi 3:4, 5
Mac. 26:5Mac 22:3
Mac. 26:6Mac 24:15
Mac. 26:7Mac 24:20, 21
Mac. 26:10Yoh 16:2; Mac 8:3; 1Ak 15:9; Aga 1:13; 1Ti 1:13
Mac. 26:10Mac 9:1, 2, 14
Mac. 26:13Mac 9:3-5; 22:6-8
Mac. 26:16Mac 22:14, 15; Aga 1:11, 12; 1Ti 1:12
Mac. 26:17Mac 22:21; Aro 11:13
Mac. 26:18Yes 61:1
Mac. 26:18Akl 1:13
Mac. 26:18Yoh 8:12; 2Ak 4:6
Mac. 26:18Aef 2:1, 2
Mac. 26:181Yo 3:5
Mac. 26:20Mac 9:22
Mac. 26:20Mac 9:28
Mac. 26:20Mt 3:8
Mac. 26:21Mac 21:30, 31
Mac. 26:22Lu 24:27, 44; Aro 3:21
Mac. 26:23Sl 22:7; 35:19; Yes 50:6; 53:5
Mac. 26:23Sl 16:10
Mac. 26:23Sl 18:49; Yes 11:10; Lu 2:30-32
Mac. 26:26Yoh 18:20
Mac. 26:31Mac 23:26, 29; 25:24, 25
Mac. 26:32Mac 25:11, 12
  • Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
  • Werengani mu Baibulo la Dziko Latsopano
  • 1
  • 2
  • 3
  • 4
  • 5
  • 6
  • 7
  • 8
  • 9
  • 10
  • 11
  • 12
  • 13
  • 14
  • 15
  • 16
  • 17
  • 18
  • 19
  • 20
  • 21
  • 22
  • 23
  • 24
  • 25
  • 26
  • 27
  • 28
  • 29
  • 30
  • 31
  • 32
Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika
Machitidwe 26:1-32

Machitidwe a Atumwi

26 Agiripa+ anauza Paulo kuti: “Ukhoza kulankhula mbali yako.” Ndiyeno Paulo anakweza dzanja nʼkuyamba kulankhula modziteteza kuti:

2 “Inu Mfumu Agiripa, ndine wosangalala kuti lero ndidziteteza pamaso panu, pa zinthu zonse zimene Ayuda akundineneza.+ 3 Makamaka chifukwa chakuti ndinu katswiri pa miyambo yonse komanso pa zimene Ayuda amakangana. Choncho ndikukupemphani kuti mundimvetsere moleza mtima.

4 Ndithudi, moyo umene ndakhala kuyambira ndili mnyamata, pakati pa anthu a mtundu wanga ndiponso mu Yerusalemu, ndi wodziwika bwino kwa Ayuda onse+ 5 amene akundidziwa kuyambira kale. Atafuna, angandichitire umboni kuti ndinalidi Mfarisi+ wa mʼgulu limene limalambira mokhwimitsa zinthu kwambiri.+ 6 Koma tsopano ndikuimbidwa mlandu chifukwa cha chiyembekezo cha zimene Mulungu analonjeza makolo athu.+ 7 Mafuko athu 12 akuyembekezera kuona kukwaniritsidwa kwa lonjezo limeneli ndipo akumuchitira Mulunguyo utumiki wopatulika mosalekeza masana ndi usiku. Choncho Mfumu, Ayuda akundiimba mlandu chifukwa cha chiyembekezo chimenechi.+

8 Nʼchifukwa chiyani anthu inu mukuona kuti nʼzosatheka kuti Mulungu aukitse akufa? 9 Inetu ndinkaganiza kuti ndiyenera kuchita zambiri zotsutsana ndi dzina la Yesu wa ku Nazareti. 10 Ndipo izi ndi zimene ndinachitadi ku Yerusalemu. Ndinkatsekera mʼndende oyera ambiri+ nditapatsidwa mphamvu ndi ansembe aakulu.+ Akaweruzidwa kuti aphedwe, ine ndinkavomereza. 11 Nthawi zambiri ndinkawapatsa chilango mʼmasunagoge onse, pofuna kuwakakamiza kuti asiye zimene amakhulupirira. Popeza ndinali nditakwiya nawo kwambiri, ndinafika powazunza ngakhale mʼmizinda yakunja.

12 Ndili ndi zolinga zimenezi, ndinanyamuka ulendo wopita ku Damasiko nditapatsidwa mphamvu komanso chilolezo ndi ansembe aakulu. 13 Koma ndili mʼnjira dzuwa lili pamutu, inu mfumu, ndinaona kuwala kochokera kumwamba koposa kuwala kwa dzuwa ndipo kunandizungulira ineyo ndiponso anthu amene ndinali nawo pa ulendowu.+ 14 Ndiyeno tonse titagwa pansi, ndinamva mawu akundiuza mʼChiheberi kuti, ‘Saulo! Saulo! Nʼchifukwa chiyani ukundizunza? Ukungovutika popitiriza kuchita ngati nyama imene ikuponya miyendo yake nʼkumamenya zisonga zotosera.’* 15 Koma ine ndinati: ‘Ambuye, ndinu ndani kodi?’ Ndipo Ambuye anati: ‘Ndine Yesu amene iwe ukumuzunza. 16 Komabe dzuka ndipo uimirire. Ndaonekera kwa iwe kuti ndikusankhe kuti ukhale mtumiki komanso mboni ya zinthu zonse zokhudza ine, zomwe waona ndiponso zimene ndidzakuonetsa.+ 17 Ndipo ndidzakupulumutsa kwa anthu awa komanso kwa anthu a mitundu ina kumene ndikukutumiza+ 18 kuti ukatsegule maso awo,+ kuwachotsa mumdima+ nʼkuwapititsa kowala+ ndiponso kuwachotsa mʼmanja mwa Satana+ nʼkuwapititsa kwa Mulungu. Ukachite zimenezi kuti machimo awo akhululukidwe+ nʼkulandira cholowa pamodzi ndi oyeretsedwa chifukwa chondikhulupirira.’

19 Choncho, Mfumu Agiripa, ine ndinaona kuti ndimvere zimene ndinaona mʼmasomphenya akumwambawo. 20 Kuyambira kwa anthu a ku Damasiko,+ kenako a ku Yerusalemu+ ndipo kenako mʼdziko lonse la Yudeya ndi anthu a mitundu ina, ndinafikitsa uthenga wakuti alape nʼkuyamba kulambira Mulungu pochita zinthu zosonyeza kulapa.+ 21 Nʼchifukwa chake Ayuda anandigwira mʼkachisi nʼkumafuna kundipha.+ 22 Komabe, popeza ndinaona Mulungu akundithandiza, ndikuchitirabe umboni kwa anthu otchuka ndiponso anthu wamba mpaka lero. Sindikunena chilichonse, koma zokhazo zimene aneneri ndi Mose ananena kuti zichitika.+ 23 Zoti Khristu adzavutika,+ ndipo monga woyamba kuukitsidwa,+ adzalalikira kwa anthu awa ndiponso kwa anthu a mitundu ina zokhudza kuwala.”+

24 Pamene Paulo ankanena zimenezi podziteteza, Fesito ananena mokweza mawu kuti: “Wachita misala iwe Paulo! Kuphunzira kwambiri kwakupengetsa!” 25 Koma Paulo anati: “Wolemekezeka a Fesito, inetu sindinachite misala, koma ndikulankhula mawu a choonadi ndipo ndili bwinobwino. 26 Kunena zoona, ndikulankhula momasuka chifukwa mfumu imene ndikulankhula nayo ikudziwa bwino zimenezi. Sindikukayikira kuti palibe ngakhale chimodzi mwa zinthu zimenezi, chimene simukuchidziwa chifukwa zimenezi sizinachitike mwamseri.+ 27 Kodi inuyo, Mfumu Agiripa, mumakhulupirira zimene aneneri analemba? Ndikudziwa kuti mumazikhulupirira.” 28 Koma Agiripa anauza Paulo kuti: “Pa nthawi yochepa ukhoza kundikopa kuti ndikhale Mkhristu.” 29 Ndiyeno Paulo anati: “Kaya pa nthawi yochepa kapena yaitali, pemphero langa kwa Mulungu ndi lakuti, onse amene andimvetsera lero, osati inu nokha, akhale ngati ine kupatulapo maunyolo okhawa.”

30 Kenako mfumu inaimirira. Bwanamkubwa, Berenike ndiponso amuna amene anakhala nawo pamodzi nawonso anaimirira. 31 Koma pochoka anayamba kukambirana kuti: “Munthu uyu sanachite chilichonse choyenera kuphedwa kapena kumangidwa.”+ 32 Ndipo Agiripa anauza Fesito kuti: “Akanakhala kuti sanapemphe kukaonekera kwa Kaisara, munthu ameneyu akanamasulidwa.”+

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena