Yakobo
5 Tamverani tsopano inu anthu achuma.+ Lirani, fuulani chifukwa cha masautso amene akubwera kwa inu.+ 2 Chuma chanu chawola, ndipo malaya anu akunja adyedwa ndi njenjete.*+ 3 Golide ndi siliva wanu wadyedwa ndi dzimbiri, ndipo dzimbiri limenelo lidzakhala umboni wokutsutsani. Lidzadya mnofu wa matupi anu. Zimene mwaunjika+ m’masiku otsiriza+ zili ngati moto.+ 4 Tamverani! Malipiro a anthu amene anagwira ntchito+ yokolola m’minda yanu, amene inu simunapereke,+ akufuula ndipo kufuula kwa okololawo kofuna thandizo+ kwafika m’makutu+ a Yehova wa makamu. 5 Mwalidyerera dziko lapansi ndipo mwasangalala.+ Mwanenepetsa mitima yanu pa tsiku lokaphedwa.+ 6 Mwaweruza ndi kupha munthu wolungama. Iye akukutsutsani.+
7 Choncho lezani mtima abale, kufikira kukhalapo*+ kwa Ambuye. Ganizirani mmene amachitira mlimi. Iye amayembekezerabe zipatso zofunika kwambiri zotuluka m’nthaka. Amakhala wodekha mpaka itagwa mvula yoyamba ndi mvula yomaliza.+ 8 Nanunso khalani oleza mtima.+ Limbitsani mitima yanu, chifukwa kukhalapo kwa Ambuye kwayandikira.+
9 Musamang’ung’udzirane abale, kuopera kuti mungaweruzidwe.+ Taonani, Woweruza waima pakhomo.+ 10 Abale, pa nkhani ya kumva zowawa+ ndi kuleza mtima,+ tengerani chitsanzo+ kwa aneneri+ amene analankhula m’dzina la Yehova.+ 11 Monga mmene mukudziwira, anthu amene anapirira timawatcha odala.+ Munamva za kupirira kwa Yobu+ ndipo mwaona zimene Yehova anamupatsa,+ mwaona kuti Yehova ndi wachikondi chachikulu ndi wachifundo.+
12 Koma koposa zonse abale anga, lekani kulumbira, kaya motchula kumwamba kapena dziko lapansi kapena lumbiro lina lililonse.+ Koma tangotsimikizani kuti mukati Inde akhaledi Inde ndipo mukati Ayi akhaledi Ayi, kuti musaweruzidwe.+
13 Kodi pali aliyense mwa inu amene akumva zowawa? Apitirize kupemphera.+ Kodi pali wina amene akukondwa? Aimbe nyimbo zotamanda Mulungu.+ 14 Kodi pali wina amene akudwala pakati panu?+ Aitane akulu a mpingo,+ ndipo iwo amupempherere ndi kumupaka mafuta+ m’dzina la Yehova. 15 Pemphero lachikhulupiriro lidzachiritsa wodwalayo,+ ndipo Yehova adzamulimbitsa.+ Ndiponso ngati anachita machimo, adzakhululukidwa.+
16 Choncho muululirane machimo anu poyera+ ndi kupemphererana, kuti muchiritsidwe.+ Pembedzero la munthu wolungama limagwira ntchito mwamphamvu kwambiri.+ 17 Eliya anali munthu monga ife tomwe,+ komabe anapemphera kuti mvula isagwe,+ ndipo mvula sinagwe kumeneko kwa zaka zitatu ndi miyezi 6. 18 Anapempheranso, ndipo mvula inagwa kuchokera kumwamba. Nthaka inatulutsa zipatso zake.+
19 Abale anga, ngati wina mwa inu wasocheretsedwa pa choonadi wina n’kumubweza,+ 20 dziwani kuti amene wabweza wochimwa panjira yake yoipa,+ adzapulumutsa moyo wa wochimwayo ku imfa+ ndipo adzakwirira machimo ambiri.+